Salimo 83:1-18

Nyimbo ndi Salimo la Asafu.+ 83  Inu Mulungu, musakhale chete.+Musakhale phee osalankhulapo kanthu ndipo musakhale duu osachitapo kanthu, inu Mulungu.+   Taonani! Adani anu akuchita phokoso.+Anthu odana nanu kwambiri atukula mitu yawo.+   Iwo amakumana mwachinsinsi kuti akambirane zochitira chiwembu anthu anu.+Ndipo amakonzera chiwembu anthu anu obisika.+   Iwo anena kuti: “Bwerani tiwafafanize kuti asakhalenso mtundu,+Ndi kuti dzina la Isiraeli lisakumbukikenso.”+   Pakuti ndi mtima wonse, iwo amagawana nzeru,+Ndipo anapangana pangano lotsutsana ndi inu.+   Amenewa ndi anthu okhala m’mahema a Edomu+ ndi m’mahema a Isimaeli, Amowabu+ ndi Ahagara,+   Agebala, Aamoni,+ Aamaleki,Afilisiti+ pamodzi ndi anthu a ku Turo.+   Asuri nawonso agwirizana nawo,+Ndipo amapereka thandizo kwa ana aamuna a Loti.+ [Seʹlah.]   Muwachitire zimene munachitira Midiyani+ ndi Sisera.+Muwachitirenso zimene munachitira Yabini+ kuchigwa cha Kisoni.+ 10  Iwo anawonongedwa ku Eni-dori.+Anasanduka manyowa a m’nthaka.+ 11  Atsogoleri awo muwachititse kukhala ngati Orebi ndi Zeebi.+Ndipo mafumu awo onse muwachititse kukhala ngati Zeba ndi Zalimuna.+ 12  Iwo anena kuti: “Tiyeni tilande malo amene Mulungu amakhalako kuti akhale athu.”+ 13  Inu Mulungu wanga, achititseni kukhala ngati udzu wouma wouluzika ndi mphepo,+Ngati mapesi otengeka ndi mphepo.+ 14  Mofanana ndi moto wotentha nkhalango,+Ndiponso malawi a moto woyaka m’mapiri,+ 15  Muwathamangitse ndi mphepo yanu yamphamvu,+Ndipo muwasokoneze ndi mphepo yanu yamkuntho.+ 16  Achititseni manyazi,+Kuti anthu afunefune dzina lanu, inu Yehova.+ 17  Achite manyazi ndi kusokonezeka nthawi zonse.+Athedwe nzeru ndi kutheratu,+ 18  Kuti anthu adziwe+ kuti inu, amene dzina lanu ndinu Yehova,+Inu nokha ndinu Wam’mwambamwamba,+ wolamulira dziko lonse lapansi.+

Mawu a M'munsi