Salimo 82:1-8

Nyimbo ya Asafu. 82  Mulungu waima pakati pa msonkhano wake,+Ndipo akuweruza pakati pa milungu kuti:+   “Kodi mudzaweruza mopanda chilungamo,+Ndi kukondera anthu oipa kufikira liti?+ [Seʹlah.]   Chitirani chilungamo anthu onyozeka ndi ana amasiye.*+Chitirani chilungamo anthu osautsika ndi osauka.+   Pulumutsani munthu wonyozeka ndi wosauka.+Alanditseni m’manja mwa anthu oipa.”+   Milunguyo siikudziwa kanthu ndipo siikuzindikira.+Ikuyendayenda mu mdima,+Ndipo maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.+   “Ine ndanena kuti, ‘Inu ndinu milungu,+Ndipo nonsenu ndinu ana a Wam’mwambamwamba.+   Ndithudi, mudzafa mmene anthu onse amafera.+Ndipo mudzagwa mmene kalonga aliyense amagwera!’”+   Nyamukani inu Mulungu, weruzani dziko lapansi.+Pakuti inu nokha muyenera kutenga mitundu yonse kukhala yanu.+

Mawu a M'munsi

Mawu ake enieni, “ana aamuna opanda bambo.”