Salimo 26:1-12

Salimo la Davide. 26  Ndiweruzeni,+ inu Yehova, pakuti ine ndayenda mogwirizana ndi mtima wanga wosagawanika,+Ndipo ndikudalira Yehova kuti ndisagwedezeke.+   Ndisanthuleni, inu Yehova, ndi kundiyesa.+Yengani impso zanga ndi mtima wanga.+   Pakuti kukoma mtima kwanu kosatha kuli pamaso panga.Ine ndayenda m’choonadi chanu.+   Sindinakhale pansi pamodzi ndi anthu achinyengo.+Ndipo sindinayanjane ndi anthu obisa umunthu wawo.+   Ndimadana ndi mpingo wa anthu ochita zoipa,+Ndipo sindikhala pansi ndi anthu oipa.+   Ndidzasamba m’manja mwanga kusonyeza kuti ndine wopanda cholakwa,+Ndipo ndidzayenda mozungulira guwa lanu lansembe, inu Yehova,+   Kuti mawu anga oyamikira amveke kwambiri,+Ndi kulengeza ntchito zanu zonse zodabwitsa.+   Yehova, ine ndimakonda nyumba imene inu mumakhala+Ndi malo amene kumakhala ulemerero wanu.+   Musachotse moyo wanga pamodzi ndi anthu ochimwa,+Kapena pamodzi ndi anthu a mlandu wamagazi.+ 10  M’manja mwa anthu amenewa muli khalidwe lotayirira,+Ndipo m’dzanja lawo lamanja mwadzaza ziphuphu.+ 11  Koma ine ndidzayenda mogwirizana ndi mtima wanga wosagawanika.+Ndiwomboleni+ ndi kundikomera mtima.+ 12  Phazi langa lidzaimadi pamalo athyathyathya.+Pamsonkhano, ndidzatamanda Yehova.+

Mawu a M'munsi