Salimo 78:1-72

Masikili.* Salimo la Asafu.+ 78  Inu anthu anga, mvetserani chilamulo changa.+Tcherani khutu ku mawu a pakamwa panga.+   Ndidzatsegula pakamwa panga ndi kunena mwambi.+Ndidzanena mawu ophiphiritsa akalekale,+   Amene tinamva ndipo tikuwadziwa,+Komanso amene makolo athu anatifotokozera.+   Mbadwa zawo sitikuzibisira mawu ophiphiritsawa,+Ndipo tidzawasimba ngakhale ku mibadwo ya m’tsogolo.+Tidzasimba ntchito zotamandika za Yehova ndi mphamvu zake,+Komanso zinthu zodabwitsa zimene wachita.+   Mulungu anaika chikumbutso pakati pa ana a Yakobo,+Iye anaika chilamulo mu Isiraeli,+Zinthu zimene analamula makolo athu,+Kuti auze ana awo.+   Kuti m’badwo wa m’tsogolo, ana amene adzabadwe m’tsogolo, adzadziwe zimenezi,+Kuti nawonso adzanyamuke ndi kusimbira ana awo.+   Kuti anawo azidzadalira Mulungu,+Ndi kuti asadzaiwale zochita za Mulungu+ koma kuti azidzasunga malamulo ake.+   Ndipo asadzakhale ngati makolo awo,+M’badwo wosamva ndi wopanduka,+M’badwo umene sunakonze mtima wawo,+Ndipo maganizo awo sanali okhulupirika kwa Mulungu.+   Ana a Efuraimu, ngakhale kuti anali ndi mivi ndi mauta,+Anathawa pa tsiku lankhondo.+ 10  Iwo sanasunge pangano la Mulungu,+Ndipo anakana kutsatira chilamulo chake.+ 11  Iwo anayambanso kuiwala zochita zake,+Ndi ntchito zake zodabwitsa zimene anawaonetsa.+ 12  Mulungu anachita zodabwitsa pamaso pa makolo awo+M’dziko la Iguputo,+ m’dera la Zowani.+ 13  Iye anagawa nyanja kuti iwo awoloke,+Ndipo anaimitsa madzi kukhala ngati khoma.+ 14  Iye anapitiriza kuwatsogolera ndi mtambo masana,+Ndipo usiku wonse anali kuwatsogolera ndi kuwala kwa moto.+ 15  Iye anang’amba miyala m’chipululu+Kuti awapatse madzi akumwa ochuluka ngati a m’nyanja.+ 16  Iye anatulutsa madzi ambiri pathanthwe,+Ndipo anachititsa madzi kutsika ngati mitsinje.+ 17  Koma iwo anapitiriza kumuchimwira+Mwa kupandukira Wam’mwambamwamba m’dera lopanda madzi.+ 18  Iwo anapitiriza kuyesa Mulungu m’mitima yawo+Mwa kupempha chakudya china chimene mtima wawo unalakalaka.+ 19  Pamenepo anayamba kulankhula mawu oipa kwa Mulungu.+Iwo anati: “Kodi Mulungu angathe kutipatsa chakudya m’chipululu muno?”+ 20  Taonani! Kodi Mulungu si uja anamenya thanthwe+Kuti madzi atuluke, kutinso patuluke mitsinje yodzaza madzi?+Koma iwo anati: “Kodi angathenso kutipatsa chakudya,+Kapena kodi angakonzere anthu ake chakudya?”+ 21  Choncho Yehova anamva zimenezo ndipo anakwiya.+Moti moto unayakira Yakobo,+Ndipo mkwiyo unatsikira pa Isiraeli.+ 22  Pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu.+Sanakhulupirire kuti iye adzawapulumutsa.+ 23  Pamenepo Mulungu analamula mitambo ya m’mlengalenga,Ndipo anatsegula zitseko zakumwamba.+ 24  Ndipo anapitiriza kuwagwetsera mana ngati mvula kuti adye.+Iye anawapatsa tirigu wochokera kumwamba.+ 25  Anthu anadya chakudya cha amphamvu.+Iye anawatumizira chakudya chokwanira.+ 26  Anachititsa mphepo ya kum’mawa kuwomba m’mlengalenga,+Ndipo mwa mphamvu zake anachititsa mphepo ya kum’mwera kuwomba.+ 27  Iye anagwetsa chakudya pa iwo ngati fumbi.+Anawagwetsera zolengedwa zamapiko zouluka, zochuluka ngati mchenga wakunyanja.+ 28  Anapitiriza kuwagwetsera zimenezi mumsasa wake,+Kuzungulira mahema ake onse.+ 29  Iwo anadya ndi kukhuta kwambiri.+Iye anawabweretsera zimene anali kulakalaka.+ 30  Iwo anafunabe chakudya china,Pamene china chinali m’kamwa.+ 31  Nthawi yomweyo, mkwiyo wa Mulungu unatsikira pa iwo.+Iye anayamba kupha anthu awo amphamvu.+Ndipo anakomola anyamata a mu Isiraeli. 32  Ngakhale zinali choncho, iwo anawonjezera machimo awo,+Ndipo sanakhulupirire ntchito zake zodabwitsa.+ 33  Choncho anathetsa masiku a moyo wawo ngati mpweya wotuluka m’mphuno.+Anadula zaka za moyo wawo ndi masoka. 34  Nthawi zonse akayamba kuwapha, iwo anali kumufunafuna.+Anali kutembenuka ndi kuyamba kufunafuna Mulungu.+ 35  Iwo anali kukumbukira kuti Mulungu anali Thanthwe lawo,+Ndiponso kuti Mulungu Wam’mwambamwamba anali Wowabwezerera.+ 36  Koma iwo anali kufuna kum’pusitsa ndi pakamwa pawo.+Ndi lilime lawo anali kufuna kunena bodza kwa iye.+ 37  Mtima wawo sunali wokhulupirika kwa iye.+Ndipo iwo sanakhulupirike ku pangano lake.+ 38  Koma anawamvera chifundo.+ Anali kukhululukira* machimo awo+ ndipo sanali kuwawononga.+Nthawi zambiri anali kubweza mkwiyo wake,+Ndipo sanali kuwasonyeza ukali wake wonse. 39  Iye anali kukumbukira nthawi zonse kuti iwo ndi anthu athupi la nyama,+Anali kukumbukira kuti moyo wawo umachoka ndipo subwereranso.+ 40  Iwo analitu kumupandukira kawirikawiri m’chipululu,+Anali kumukhumudwitsa m’chipululumo!+ 41  Mobwerezabwereza, anali kumuyesa Mulungu,+Ndipo anali kumvetsa chisoni Woyera wa Isiraeli.+ 42  Iwo sanakumbukire dzanja la Mulungu,+Sanakumbukire tsiku limene anawawombola kwa mdani wawo,+ 43  Iwo sanakumbukire mmene anaikira zizindikiro zake mu Iguputo,+Ndi zozizwitsa zimene anachita m’dera la Zowani,+ 44  Mmene anasinthira mitsinje ing’onoing’ono yotuluka mumtsinje wa Nailo kukhala magazi,+Moti sanathe kumwa madzi ake.+ 45  Mulungu anawatumizira tizilombo toyamwa magazi kuti tiwadye,+Ndi achule kuti awawononge.+ 46  Anapereka zokolola zawo kwa mphemvu,Ndipo ntchito yawo yolemetsa anaipereka kwa dzombe.+ 47  Anapha mitengo yawo ya mpesa ndi mvula yamatalala.+Anapha mitengo yawo ya mkuyu ndi matalala.+ 48  Anaphanso nyama zawo zonyamula katundu ndi matalala,+Ndiponso ziweto zawo ndi mliri wakupha. 49  Anawasonyeza mkwiyo wake woyaka moto,+Ukali, ziweruzo zamphamvu ndi masautso.+Anawatumizira makamu a angelo obweretsa masoka.+ 50  Mkwiyo wake anaulambulira njira.+Sanawabweze kuwachotsa ku imfa.Ndipo anawapha ndi mliri.+ 51  Pamapeto pake anapha ana onse oyamba kubadwa mu Iguputo,+Amene ndi chiyambi cha mphamvu zawo zobereka m’mahema a Hamu.+ 52  Kenako anachititsa anthu ake kuchoka m’dzikolo ngati gulu la nkhosa,+Anawayendetsa m’chipululu ngati gulu la ziweto.+ 53  Anapitiriza kuwatsogolera ndi kuwateteza ndipo iwo sanachite mantha.+Nyanja inamiza adani awo.+ 54  Kenako anawalowetsa m’dziko lake lopatulika,+M’dera lamapiri ili limene dzanja lake lamanja linatenga.+ 55  Chifukwa cha iwo anachotsa mitundu ina pang’onopang’ono m’dzikoli,+Ndipo anayesa dzikoli ndi kuligawa kwa iwo kukhala cholowa chawo,+Moti anachititsa mafuko a Isiraeli kukhala m’nyumba zawozawo.+ 56  Koma iwo anayamba kuyesa Mulungu Wam’mwambamwamba ndi kum’pandukira,+Ndipo sanasunge zikumbutso zake.+ 57  Iwo anali kubwerera ndi kuchita zinthu mwachinyengo ngati makolo awo.+Anapotoka maganizo ngati uta wosakunga kwambiri.+ 58  Iwo anapitiriza kumukhumudwitsa ndi malo awo okwezeka,+Ndipo anamuchititsa nsanje ndi zifaniziro zawo zogoba.+ 59  Mulungu anamva+ ndipo anakwiya kwambiri.+Chotero ananyansidwa kwambiri ndi Isiraeli.+ 60  Pamapeto pake anasiya chihema chopatulika cha ku Silo,+Hema limene anali kukhalamo pakati pa anthu ochokera kufumbi.+ 61  Analola kuti chizindikiro cha mphamvu zake chitengedwe ndi adani ake,+Iye analola kuti chizindikiro cha kukongola kwake chikhale m’manja mwa adani.+ 62  Iye anapereka anthu ake ku lupanga,+Ndipo anakwiyira cholowa chake.+ 63  Anyamata ake ananyeka ndi moto,Ndipo anamwali ake sanatamandidwe.+ 64  Ansembe ake anagwa ndi lupanga,+Ndipo akazi awo amasiye sanalire.+ 65  Pamenepo Yehova anagalamuka ngati akudzuka kutulo,+Ngati munthu wamphamvu amene akugalamuka pambuyo pomwa vinyo wambiri.+ 66  Iye anathamangitsa adani ake ndi kuwapha.+Anawachititsa kuti akhale akutonzedwa mpaka kalekale.+ 67  Iye anakana hema wa Yosefe,+Ndipo sanasankhe fuko la Efuraimu.+ 68  Koma anasankha fuko la Yuda,+Phiri la Ziyoni limene analikonda.+ 69  Anayamba kumanga malo opatulika ngati malo okwera a paphiri,+Ngati dziko lapansi limene analikhazikitsa mpaka kalekale.+ 70  Choncho anasankha Davide mtumiki wake,+Ndipo anamuchotsa kumakola a nkhosa.+ 71  Anamutenga kumene anali kuweta nkhosa zoyamwitsa,+Anamutenga kuti akhale m’busa wa ana a Yakobo amene ndi anthu ake,+Ndi Isiraeli, amene ndi cholowa chake.+ 72  Iye anayamba kuwaweta malinga ndi mtima wake wosagawanika,+Ndipo anayamba kuwatsogolera mwaluso.+

Mawu a M'munsi

Onani mawu a m’munsi pa Sl 32:Kamutu.
Mawu ake enieni, “kuphimba.”