Salimo 44:1-26

Kwa wotsogolera nyimbo. Salimo la ana a Kora.+ Masikili.* 44  Inu Mulungu, ife tamva ndi makutu athu,Makolo athu anatifotokozera+Ntchito zimene inu munachita m’masiku awo,+M’masiku akale.+   Munapitikitsa anthu a mitundu ina ndi dzanja lanu,+Ndipo m’malo mwawo munakhazikitsa anthu anu.+Munagonjetsa mitundu ya anthu ndi kuipitikitsa.+   Pakuti iwo sanatenge dzikolo chifukwa cha lupanga lawo,+Ndipo si mkono wawo umene unawabweretsera chipulumutso.+Koma chinabwera ndi dzanja lanu lamanja,+ mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu,Chifukwa munakondwera nawo.+   Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga.+Lamulani kuti Yakobo alandire chipulumutso chachikulu.+   Ndi thandizo lanu tidzakankha adani athu.+M’dzina lanu tidzapondereza amene akutiukira.+   Pakuti sindinadalire uta wanga,+Ndipo si lupanga langa limene linandipulumutsa.+   Ndinu amene munatipulumutsa kwa adani athu,+Ndipo munanyazitsa anthu amene amadana nafe kwambiri.+   Tidzayamika Mulungu nthawi zonse,+Tidzatamanda dzina lanu mpaka kalekale.+ [Seʹlah.]   Koma tsopano mwatitaya ndi kutichititsa manyazi,+Simukuyenda ndi magulu athu ankhondo.+ 10  Mwachititsa kuti tithawe pamaso pa adani athu,+Ndipo anthu odana nafe kwambiri afunkha zinthu zathu.+ 11  Mwatipereka kwa adani athu kuti atidye ngati nkhosa,+Ndipo mwatimwaza pakati pa anthu a mitundu ina.+ 12  Mwagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika kwambiri,+Ndipo simunapeze phindu ndi mtengo wawo. 13  Mwatisandutsa chitonzo kwa anthu oyandikana nafe,+Mwatisandutsa chinthu chonyozeka ndi choseketsa kwa onse otizungulira.+ 14  Mwatisandutsa mwambi pakati pa anthu a mitundu ina,+Mwatisandutsa anthu amene anthu a mitundu inawo akuwapukusira mitu.+ 15  Zondichititsa manyazi zili pamaso panga tsiku lonse,Ndipo manyazi aphimba nkhope yanga,+ 16  Chifukwa cha mawu a munthu wonditonza ndi wolankhula zachipongwe,Ndiponso chifukwa cha mdani wanga ndi wofuna kundibwezera choipa.+ 17  Zonsezi ndi zimene zatigwera, koma sitinakuiwaleni,+Sitinachite mwachinyengo ndi pangano lanu.+ 18  Mitima yathu sinakhale yosakhulupirika n’kuchoka panjira yanu,+Ndipo mapazi athu sanapatuke panjira yanu.+ 19  Pakuti inu mwatiphwanya kumalo amene mimbulu imasonkhana,+Mwatiphimba ndi mdima wandiweyani.+ 20  Ngati tikanaiwala dzina la Mulungu wathu,Kapena kupemphera kwa mulungu wachilendo titakweza manja athu,+ 21  Kodi Mulungu sakanafufuza zimenezi?+Pakuti iye amadziwa zinsinsi za mumtima.+ 22  Koma chifukwa cha inu, tikuphedwa nthawi zonse.Takhala ngati nkhosa zokaphedwa.+ 23  Nyamukani. N’chifukwa chiyani mukugonabe, inu Yehova?+Dzukani. Musatitaye kwamuyaya.+ 24  N’chifukwa chiyani mukubisabe nkhope yanu?N’chifukwa chiyani mukuiwala masautso athu ndi kuponderezedwa kwathu?+ 25  Pakuti miyoyo yathu yasautsika.+Mimba zathu zili thasa! padothi. 26  Nyamukani kuti mutithandize+Tiwomboleni chifukwa cha kukoma mtima kwanu kosatha.+

Mawu a M'munsi

Onani mawu a m’munsi pa Sl 32:Kamutu.