Salimo 86:1-17

Pemphero la Davide. 86  Tcherani khutu inu Yehova. Ndiyankheni,+Pakuti ndasautsika ndipo ndasauka.+   Tetezani moyo wanga pakuti ndine wokhulupirika.+Inu ndinu Mulungu wanga, pulumutsani mtumiki wanu amene amakukhulupirirani.+   Ndikomereni mtima inu Yehova,+Pakuti ndimaitana inu tsiku lonse.+   Sangalatsani mtima wa ine mtumiki wanu,+Pakuti ndapereka moyo wanga kwa inu Yehova.+   Pakuti inu Yehova ndinu Mulungu wabwino+ ndipo ndinu wokonzeka kukhululuka.+Kukoma mtima kosatha kumene mumawasonyeza onse oitana pa inu ndi kwakukulu.+   Inu Yehova, tcherani khutu ku pemphero langa.+Ndipo mvetserani mawu a kuchonderera kwanga.+   Pa tsiku la nsautso yanga ndidzaitana pa inu,+Ndipo inu mudzandiyankha.+   Inu Yehova, palibe mulungu wina amene angafanane ndi inu.+Ndipo palibe ntchito zilizonse zofanana ndi ntchito zanu.+   Mitundu yonse imene munapanga idzabwera kwa inu,+Ndipo idzagwada pamaso panu, inu Yehova,+Ndi kulemekeza dzina lanu.+ 10  Pakuti inu ndinu wamkulu ndipo mukuchita zinthu zodabwitsa.+Inu nokha ndinu Mulungu.+ 11  Inu Yehova, ndilangizeni za njira yanu.+Ndidzayenda m’choonadi chanu.+Ndipatseni mtima wosagawanika kuti ndiope dzina lanu.+ 12  Ndikukutamandani inu Yehova Mulungu wanga ndi mtima wanga wonse,+Ndipo ndidzalemekeza dzina lanu mpaka kalekale, 13  Pakuti kukoma mtima kosatha kumene mwandisonyeza ndi kwakukulu,+Ndipo mwapulumutsa moyo wanga ku Manda, kumalo apansi penipeni.+ 14  Inu Mulungu, anthu odzitukumula andiukira.+Khamu la anthu opondereza anzawo likufunafuna moyo wanga,+Ndipo sanakuikeni patsogolo pawo.+ 15  Koma inu Yehova, ndinu Mulungu wachifundo ndi wachisomo,+Wosakwiya msanga+ ndiponso wodzaza ndi kukoma mtima kosatha ndi choonadi.+ 16  Ndicheukireni ndi kundikomera mtima.+Patsani mtumiki wanu mphamvu,+Ndipo pulumutsani mwana wa kapolo wanu wamkazi.+ 17  Ikani chizindikiro cha ubwino wanu pa ine,Kuti anthu odana nane aone zimenezi ndi kuchita manyazi,+Pakuti inu Yehova mwandithandiza ndi kundilimbikitsa.+

Mawu a M'munsi