Salimo 30:1-12

Nyimbo ndi Salimo la Davide lotsegulira nyumba.+ 30  Ndidzakutamandani inu Yehova, pakuti mwandipulumutsa,+Ndipo simunalole kuti adani anga akondwere ndi kusautsika kwanga.+   Inu Yehova Mulungu wanga, ndinafuulira kwa inu kuti mundithandize ndipo munandichiritsa.+   Inu Yehova, mwanditulutsa m’Manda,+Mwandisunga ndi moyo, kuti ndisatsikire m’dzenje.+   Imbani nyimbo zotamanda Yehova, inu okhulupirika ake,+Yamikani dzina lake loyera.*+   Chifukwa mkwiyo wa Mulungu sukhalitsa pa munthu,+Koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse.+Usiku kumakhala kulira,+ koma m’mawa kumakhala kufuula ndi chisangalalo.+   Mtima wanga utakhazikika ndinati:+“Sindidzagwedezeka.”+   Inu Yehova, chifukwa chakuti munandikomera mtima munakhazikitsa mwamphamvu phiri langa.+Pamene munabisa nkhope yanu, ndinasokonezeka.+   Ndinaitana inu Yehova,+Ndipo ndinachonderera Yehova kuti andikomere mtima.+   Kodi magazi anga angakhale ndi phindu lanji ngati nditatsikira kudzenje la manda?+Kodi fumbi lidzakutamandani?+ Kodi lidzalengeza kuti inu ndinu woona?+ 10  Imvani inu Yehova, ndi kundikomera mtima.+Inu Yehova, khalani mthandizi wanga.+ 11  Mwasintha kulira kwanga kuti kukhale kuvina.+Mwandivula chiguduli* changa ndipo mwandiveka chisangalalo,+ 12  Kuti mtima wanga uimbe nyimbo zokutamandani ndipo usakhale chete.+Inu Yehova Mulungu wanga, ndidzakutamandani mpaka kalekale.+

Mawu a M'munsi

Mawu ake enieni, “chikumbutso chake choyera.”
Ena amati “saka.”