Salimo 4:1-8

Kwa wotsogolera nyimbo: Nyimboyi iimbidwe ndi zipangizo za zingwe.+ Nyimbo ya Davide. 4  Ndikaitana, mundiyankhe inu Mulungu wanga wolungama.+M’masautso anga mundiimiritse pamalo otakasuka.Mundikomere mtima+ ndipo imvani pemphero langa.   Inu ana a anthu, kodi mudzandinyoza chifukwa cha ulemerero wanga+ kufikira liti?Mudzakonda zinthu zopanda pake kufikira liti?Mudzafunafuna nkhani yoti mundinamizire kufikira liti? [Seʹlah.]   Choncho dziwani kuti Yehova adzapatula wokhulupirika wake.+Yehova adzamva ndikaitana.+   Ngati mwakwiya, musachimwe.+Lankhulani mumtima mwanu, muli pabedi panu,+ ndipo mukhale chete. [Seʹlah.]   Perekani nsembe zachilungamo,+Ndipo khulupirirani Yehova.+   Pali ambiri amene akunena kuti: “Ndani adzationetsa zinthu zabwino?”Inu Yehova, tiunikeni ndi kuwala kwa nkhope yanu.+   Mudzasangalatsadi mtima wanga,+Kuposanso mmene iwo amasangalalira, mbewu ndi vinyo wawo watsopano zikachuluka.+   Ndidzagona pansi ndi kupeza tulo mu mtendere,+Pakuti inu nokha Yehova mumandichititsa kukhala wotetezeka.+

Mawu a M'munsi