Salimo 76:1-12

Kwa wotsogolera nyimbo: Iimbidwe ndi zipangizo za zingwe. Nyimbo ndi Salimo la Asafu.+ 76  Mulungu amadziwika mu Yuda.+Dzina lake ndi lalikulu mu Isiraeli.+   Malo ake opumulirako ali ku Salemu,+Malo ake okhalamo ali ku Ziyoni.+   Kumeneko wathyola mivi yoyaka moto,+Wathyola chishango, lupanga ndi zida zankhondo.+ [Seʹlah.]   Inu Mulungu, mwazunguliridwa ndi kuwala, ndipo ndinu wochititsa nthumanzi kuposa mapiri amene muli nyama zodya zinzake.+   Anthu olimba mtima alandidwa zinthu zawo,+Iwo awodzera ndi kugona tulo,+Ndipo palibe ngakhale mmodzi mwa anthu onse olimba mtimawo amene ali ndi mphamvu zotsutsa.+   Hatchi komanso wokwera galeta agona tulo tofa nato chifukwa cha kudzudzula kwanu, inu Mulungu wa Yakobo.+   Inu ndinu wochititsa mantha,+Ndani angaime pamaso panu inu mutakwiya kwambiri?+   Munachititsa ziweruzo zanu kumveka kuchokera kumwambako.+Dziko lapansi linachita mantha ndipo linakhala duu+   Pamene Mulungu ananyamuka ndi kupereka chiweruzo,+Kuti apulumutse anthu onse ofatsa padziko lapansi.+ [Seʹlah.] 10  Pakuti mkwiyo wa munthu udzakutamandani,+Mkwiyo wake wotsala mudzaumangirira m’chiuno mwanu. 11  Inu nonse amene mwazungulira Mulungu, lonjezani ndi kukwaniritsa malonjezo anuwo kwa Yehova Mulungu wanu.+Bweretsani mphatso mwamantha.+ 12  Mulungu adzatsitsa atsogoleri odzikuza.+Iye ndi wochititsa mantha kwa mafumu a padziko lapansi.+

Mawu a M'munsi