Salimo 60:1-12

Kwa wotsogolera nyimbo pa Duwa la Chikumbutso. Mikitamu.* Salimo la Davide. Nyimbo yophunzitsira.+ Pa nthawi imene Davide anali pankhondo ndi Aramu-naharaimu ndi Aramu-Zoba, ndipo Yowabu anabwerera ndi kukapha Aedomu 12,000 m’chigwa cha Mchere.+ 60  Inu Mulungu, mwatitaya, ndipo mwasokoneza magulu athu ankhondo,+Mwakwiya. Tiloleni tibwerere kwa inu.+   Mwagwedeza dziko lapansi, ndipo mwaling’amba.+Tsekani ming’alu yake, pakuti lagwedezeka.+   Anthu anu mwawaonetsa zovuta.+Mwatimwetsa vinyo ndipo tikuyenda dzandidzandi.+   Anthu okuopani mwawapatsa chizindikiro+Kuti athawe uta mokhotakhota. [Seʹlah.]   Kuti okondedwa anu apulumutsidwe,+Tipulumutseni ndi dzanja lanu lamanja ndi kutiyankha.+   Pokhala woyera, Mulungu walankhula kuti:+“Ndidzakondwa ndi kupereka Sekemu ngati gawo la cholowa.+Ndipo ndidzayezera anthu anga chigwa cha Sukoti.+   Giliyadi ndi wanga ndipo Manase ndi wanganso.+Efuraimu ndi malo otetezeka a mtsogoleri amene ine ndamuika.Yuda ndi ndodo ya mtsogoleri wanga.+   Mowabu ndi beseni langa losambiramo.+Ndidzaponyera Edomu nsapato zanga.+Ndidzafuula mosangalala chifukwa chogonjetsa Filisitiya.”+   Ndani adzandibweretsa kumzinda wozunguliridwa ndi adani?+Ndani adzanditsogolera mpaka kukafika ku Edomu?+ 10  Ndinu Mulungu amene mungatichititse kupambana! Koma onani tsopano mwatitaya,+Ndipo inu Mulungu wathu, simukupita kunkhondo pamodzi ndi magulu athu ankhondo.+ 11  Tithandizeni kuti tichoke m’masautso,+Pakuti chipulumutso chochokera kwa munthu wochokera kufumbi n’chopanda pake.+ 12  Ndi thandizo la Mulungu, tidzalandira mphamvu,+Ndipo Mulungu adzapondereza adani athu.+

Mawu a M'munsi

Onani mawu a m’munsi pa Sl 16:Kamutu.