Salimo 109:1-31

Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ndi Salimo la Davide. 109  Inu Mulungu amene ndimakutamandani,+ musakhale chete.+   Munthu woipa ndiponso munthu wachinyengo andinenera zoipa ndi pakamwa pawo.+Iwo anena za ine ndi lilime lonama.+   Andizungulira ndi mawu achidani,+Ndipo akulimbana nane popanda chifukwa.+   Ndikawasonyeza chikondi amanditsutsa,+Koma ine ndimapemphera.+   Ndikawachitira zabwino amandibwezera zoipa,+Ndikawasonyeza chikondi amandibwezera chidani.+   Muikireni woweruza woipa,Ndipo kudzanja lake lamanja kuime wotsutsana naye.+   Pamene akuweruzidwa amuweruze kuti ndi woipa.Ndipo pemphero lake likhale tchimo.+   Masiku a moyo wake akhale ochepa.+Udindo wake monga woyang’anira utengedwe ndi munthu wina.+   Ana ake akhale amasiye,*+Ndipo mkazi wakenso akhale wamasiye.+ 10  Ana ake azingoyendayenda ndithu,+Ndipo azipemphapempha.Azichoka m’mabwinja mmene akukhala, n’kupita kukafunafuna chakudya.+ 11  Wopereka ngongole yakatapira* atchere msampha pa zonse zimene ali nazo,+Ndipo anthu achilendo+ afunkhe zinthu zimene wakhetsera thukuta.+ 12  Pasapezeke womusonyeza kukoma mtima kosatha,+Ndipo pasapezeke wokomera mtima ana ake amasiyewo. 13  Mbadwa zake ziphedwe ndi kuchotsedwa m’dziko.+Dzina lawo lifafanizidwe mu m’badwo wotsatira.+ 14  Yehova akumbukire cholakwa cha makolo ake,+Ndipo tchimo la mayi ake+ lisafafanizidwe.+ 15  Tchimo ndi cholakwacho zikhale pamaso pa Yehova nthawi zonse,+Ndipo achotse dzina lawo padziko lapansi kuti lisakumbukiridwenso,+ 16  Chifukwa chakuti sanakumbukire kusonyeza kukoma mtima kosatha,+M’malomwake anapitiriza kuthamangitsa wosautsika ndi wosauka,+Komanso munthu wa mtima wachisoni kuti amuphe.+ 17  Iye anakonda kutemberera ena,+ mwakuti matemberero anabwera kwa iye.+Koma kudalitsa ena sikunali kumusangalatsa,+Moti madalitso anali patali ndi iye,+ 18  Iye anali kuvala matemberero ngati chovala.+Matembererowo analowa mwa iye ngati madzi,+Ndiponso analowa m’mafupa ake ngati mafuta. 19  Kwa iye matembererowo akhale ngati chovala chimene amadziphimba nacho,+Komanso ngati lamba amene amamanga m’chiuno mwake nthawi zonse.+ 20  Amenewa ndi malipiro a Yehova kwa aliyense amene amalimbana nane,+Ndi kwa amene amakamba zondichitira zinthu zoipa.+ 21  Koma inu ndinu Yehova Ambuye Wamkulu Koposa.+Ndikomereni mtima chifukwa cha dzina lanu.+Ndilanditseni,+ popeza kukoma mtima kwanu kosatha ndi kwakukulu. 22  Ine ndasautsika ndipo ndasauka,+Mtima wanga walasika mkati mwanga.+ 23  Ine ndiyenera kuchoka mofanana ndi chithunzithunzi chimene chimazimiririka dzuwa likalowa.+Ndakutumulidwa ngati dzombe. 24  Mawondo anga akugwedezeka chifukwa chosala kudya,+Ndawonda ndipo ndilibe mafuta alionse odzola.+ 25  Kwa iwo ndakhala chinthu choyenera kutonzedwa.+Akandiona amapukusa mitu yawo.+ 26  Ndithandizeni, inu Yehova Mulungu wanga.+Ndipulumutseni malinga ndi kukoma mtima kwanu kosatha.+ 27  Iwo adziwe kuti ili ndi dzanja lanu.+Adziwe kuti inu Yehova mwachita zimenezi.+ 28  Alekeni anditemberere,+Koma inu mundipatse madalitso.+Iwo aimirira kuti andiukire koma inu muwachititse manyazi,+Ndipo ine mtumiki wanu ndisangalale.+ 29  Amene akulimbana ndi ine avale manyazi,+Ndipo adziphimbe ndi manyaziwo ngati akudziphimba ndi malaya akunja odula manja.+ 30  Ndidzatamanda kwambiri Yehova ndi pakamwa panga,+Ndipo ndidzamutamanda pakati pa anthu ambiri.+ 31  Pakuti adzaima kudzanja lamanja la munthu wosauka,+Kuti am’pulumutse kwa omuweruza mopanda chilungamo.

Mawu a M'munsi

Mawu ake enieni, “ana aamuna opanda bambo.”
Onani mawu a m’munsi pa Eks 22:25.