Salimo 149:1-9

149  Tamandani Ya, anthu inu!+Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,+Muimbireni nyimbo zomutamanda mu mpingo wa anthu ake okhulupirika.+   Isiraeli asangalale ndi Womupanga Wamkulu,+Ana a Ziyoni akondwere ndi Mfumu yawo.+   Atamande dzina lake mwa kuvina.+Amuimbire nyimbo zomutamanda ndi maseche ndi zeze,+   Pakuti Yehova amasangalala ndi anthu ake.+Iye amakongoletsa anthu ofatsa ndi chipulumutso.+   Anthu okhulupirika akondwere mu ulemerero.Iwo aimbe mosangalala pamabedi awo.+   Pakamwa pawo patuluke nyimbo zotamanda Mulungu,+Ndipo lupanga lakuthwa konsekonse likhale m’manja mwawo,+   Kuti abwezere anthu a mitundu ina,+Ndi kudzudzula mitundu ya anthu,+   Ndiponso kuti amange mafumu awo maunyolo,+Ndi kumanga anthu awo olemekezeka m’matangadza achitsulo.   Kuti awaweruze motsatira chigamulo cholembedwa.+Ulemerero umenewu ndi wa anthu onse okhulupirika a Mulungu.+Tamandani Ya, anthu inu!+

Mawu a M'munsi