Mukuitanidwa
Kulambira Koyera
Msonkhano wa Mboni za Yehova wa 2025
Fufuzani Komwe Kudzachitikire Msonkhanowu Pafupi ndi Kwanu
Simudzalipira kuti mulowe komanso sikudzakhala kuyendetsa mbale ya zopereka
Zomwe Zili Pamsonkhanowu
Lachisanu: Pogwiritsa ntchito mavidiyo, mudzaona mmene moyo unalili kumadera amene Yesu anakhalako komanso kulalikirako.
Loweruka: Mudzaona mmene zomwe zinachitika kumayambiriro kwa utumiki wa Yesu, zinakwaniritsira maulosi omwe analoseredwa kalekale.
Lamlungu: Munkhani yakuti “Kodi Zomwe Mumakhulupirira Ndi Zoona?” mudzaona chifukwa chake timafunika kuganizira za zomwe timakhulupirira komanso mmene tingafufuzire choonadi.
Vidiyo
Uthenga Wabwino wa Yesu: Gawo 2 ndi 3
Yesu atabatizidwa, anakhala Mesiya kapena kuti Khristu. M’miyezi yotsatira anayesedwa ndi Mdyerekezi, anayamba kusonkhanitsa ophunzira ake komanso anachita zozizwitsa zake zoyambirira. Mudzaonera zimenezi komanso zochitika zina m’zigawo za mavidiyo a Yesu omwe adzaonetsedwe pamsonkhanowu.
Pitani pa jw.org kuti muone pulogalamu yonse komanso kuti muonere mavidiyo otsatirawa:
Kodi Pamisonkhano Yathu Ikuluikulu Pamachitika Zotani?
Onani zomwe zimachitika pamsonkhano wa Mboni za Yehova.
Msonkhano wa Mboni za Yehova wa 2025 Wakuti: “Kulambira Koyera”
Onani zina zomwe zili pamsonkhano wachaka chino.
Zimene Zili Muvidiyo Yakuti: Uthenga Wabwino wa Yesu
Kungochokera pamene anayamba utumiki wake, Yesu Khristu ankatsutsidwa ndi anthu, Mdyerekezi komanso ziwanda. Kodi zimenezi zikanamuchititsa kuti asiye kukhala wokhulupirika kwa Mulungu?