Mukuitanidwa

Kulambira Koyera

Msonkhano wa Mboni za Yehova wa 2025

Fufuzani Komwe Kudzachitikire Msonkhanowu Pafupi ndi Kwanu

Simudzalipira kuti mulowe komanso sikudzakhala kuyendetsa mbale ya zopereka

Zomwe Zili Pamsonkhanowu

Lachisanu: Pogwiritsa ntchito mavidiyo, mudzaona mmene moyo unalili kumadera amene Yesu anakhalako komanso kulalikirako.

Loweruka: Mudzaona mmene zomwe zinachitika kumayambiriro kwa utumiki wa Yesu, zinakwaniritsira maulosi omwe analoseredwa kalekale.

Lamlungu: Munkhani yakuti “Kodi Zomwe Mumakhulupirira Ndi Zoona?” mudzaona chifukwa chake timafunika kuganizira za zomwe timakhulupirira komanso mmene tingafufuzire choonadi.

Vidiyo

Uthenga Wabwino wa Yesu: Gawo 2 ndi 3

Yesu atabatizidwa, anakhala Mesiya kapena kuti Khristu. M’miyezi yotsatira anayesedwa ndi Mdyerekezi, anayamba kusonkhanitsa ophunzira ake komanso anachita zozizwitsa zake zoyambirira. Mudzaonera zimenezi komanso zochitika zina m’zigawo za mavidiyo a Yesu omwe adzaonetsedwe pamsonkhanowu.

Pitani pa jw.org kuti muone pulogalamu yonse komanso kuti muonere mavidiyo otsatirawa:

Kodi Pamisonkhano Yathu Ikuluikulu Pamachitika Zotani?

Onani zomwe zimachitika pamsonkhano wa Mboni za Yehova.

Msonkhano wa Mboni za Yehova wa 2025 Wakuti: “Kulambira Koyera”

Onani zina zomwe zili pamsonkhano wachaka chino.

Zimene Zili Muvidiyo Yakuti: Uthenga Wabwino wa Yesu

Kungochokera pamene anayamba utumiki wake, Yesu Khristu ankatsutsidwa ndi anthu, Mdyerekezi komanso ziwanda. Kodi zimenezi zikanamuchititsa kuti asiye kukhala wokhulupirika kwa Mulungu?