Mukuitanidwa
Chimwemwe Chosatha
Msonkhano wa Mboni za Yehova wa 2026
Fufuzani Komwe Kudzachitikire Msonkhanowu Pafupi ndi Kwanu
Simudzalipira kuti mulowe komanso sikudzakhala kuyendetsa mbale ya zopereka
Zomwe Zili Pamsonkhanowu
Lachisanu: Tidzaona umboni wa m’Malemba wakuti Mulungu ndi Mwana wake Yesu, amafuna kuti inuyo muzisangalala.
Loweruka: Tidzaona zimene tingachite kuti tipeze chimwemwe chosatha pokambirana zimene Yesu anaphunzitsa pa ulaliki wake wa paphiri.
Lamlungu: Munkhani yakuti “Kodi Mwapeza Chuma Chamtengo Wapatali?” mudzaona mmene choonadi cha m’Baibulo chathandizira anthu mamiliyoni kuti azikhala osangalala.
Vidiyo
Uthenga Wabwino wa Yesu: Gawo 4 mpaka 6
Tidzaona Yesu akuphunzitsa anthu ambiri, kuchiritsa odwala komanso kuukitsa akufa. Tsiku lililonse la msonkhanowu tizidzaonera gawo limodzi la mavidiyo osangalatsa komanso olimbikitsa amenewa.
Pitani pa jw.org kuti muone pulogalamu yonse komanso kuti muonere mavidiyo otsatirawa:
Kodi Pamisonkhano Yathu Ikuluikulu Pamachitika Zotani?
Onani zomwe zimachitika pamsonkhano wa Mboni za Yehova.
Onani zina zomwe zili pamsonkhano wachaka chino.
Kodi Yesu ankagwiritsira ntchito bwanji mphatso zimene anali nazo pothandiza ena?
Onerani magawo omwe anaonetsedwa pamisonkhano yapitayi.

