Salimo 121:1-8

Nyimbo Yokwerera Kumzinda. 121  Ndakweza maso anga kuyang’ana kumapiri.+Kodi thandizo langa lichokera kuti?+   Thandizo langa lichokera kwa Yehova,+Wopanga kumwamba ndi dziko lapansi.+   Iye sangalole kuti phazi lako lipunthwe.+Amene amakuyang’anira sangawodzere.+   Taonani! Amene akuyang’anira Isiraeli,+Sangawodzere kapena kugona.+   Yehova akukuyang’anira.+Yehova ndiye mthunzi wako+ kudzanja lako lamanja.+   Masana dzuwa silidzakupweteka,+Kapenanso mwezi usiku.+   Yehova adzakuteteza ku masoka onse.+Iye adzateteza moyo wako.+   Yehova adzakuteteza pa zochita zako zonse,+Kuyambira tsopano mpaka kalekale.+

Mawu a M'munsi