Salimo 112:1-10

112  Tamandani Ya, anthu inu!+ א [ʼAʹleph]Wodala ndi munthu woopa Yehova,+ב [Behth]Munthu amene amasangalala kwambiri+ ndi malamulo ake.+ ג [Giʹmel]   Ana ake adzakhala amphamvu padziko lapansi.+ ד [Daʹleth]Ndipo m’badwo wa anthu olungama udzadalitsidwa.+ ה [Heʼ]   Zinthu zamtengo wapatali ndiponso chuma zili m’nyumba yake,+ו [Waw]Ndipo chilungamo chake chidzakhalapo kwamuyaya.+ ז [Zaʹyin]   Waunika mu mdima kuti anthu owongoka mtima aone kuwala.+ ח [Chehth]Iye ndi wachisomo, wachifundo ndi wolungama.+ ט [Tehth]   Munthu wachisomo+ komanso wokongoza ena zinthu ndi wabwino.+ י [Yohdh]Amachita zinthu mwachilungamo.+ כ [Kaph]   Ndithudi munthu wotero sadzagwedezeka ngakhale pang’ono.+ ל [Laʹmedh]Wolungama adzakumbukiridwa mpaka kalekale.+ מ [Mem]   Sadzaopa uthenga woipa.+ נ [Nun]Mtima wake ndi wokhazikika,+ ndipo umadalira Yehova.+ ס [Saʹmekh]   Mtima wake sungagwedezeke,+ ndipo sadzachita mantha,+ע [ʽAʹyin]Pamapeto pake adzayang’ana adani ake atagonjetsedwa.+ פ [Peʼ]   Iye wagawira ena mowolowa manja, wapereka kwa anthu aumphawi.+ צ [Tsa·dhehʹ]Chilungamo chake chidzakhalapo kwamuyaya.+ ק [Qohph]Nyanga* yake idzakwezedwa ndi ulemerero.+ ר [Rehsh] 10  Woipa adzaona zimenezi ndipo adzasautsika.+ ש [Shin]Adzakukuta mano ndi kusungunuka.+ ת [Taw]Chikhumbo cha anthu oipa chidzatha.+

Mawu a M'munsi

Onani mawu a m’munsi pa 1Sa 2:1.