Salimo 113:1-9

113  Tamandani Ya, anthu inu!+Inu atumiki a Yehova, mutamandeni,+Tamandani dzina la Yehova.+   Dzina la Yehova lidalitsike,+Kuyambira tsopano mpaka kalekale.+   Kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera,+Dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.+   Yehova wakwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.+Ulemerero wake uli pamwamba pa kumwamba.+   Ndani angafanane ndi Yehova Mulungu wathu,+Amene amakhala pamwamba?+   Iye amatsika m’munsi kuti aone kumwamba ndi dziko lapansi.+   Amadzutsa munthu wonyozeka kumuchotsa m’fumbi.+Amakweza munthu wosauka kumuchotsa padzala,+   Kuti amukhazike pamodzi ndi anthu olemekezeka,+Pamodzi ndi anthu olemekezeka pakati pa anthu a Mulungu.+   Akuchititsa mkazi wosabereka kukhala m’nyumba+Monga mayi wosangalala wa ana aamuna.+Tamandani Ya, anthu inu!+

Mawu a M'munsi