Salimo 66:1-20

Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ndi Salimo. 66  Inu anthu nonse padziko lapansi, fuulirani Mulungu mosangalala chifukwa wapambana.+   Imbani nyimbo zotamanda dzina lake.+M’patseni ulemerero ndi kumutamanda.+   Muuzeni Mulungu kuti: “Ntchito zanu ndi zochititsadi mantha!+Chifukwa cha kuchuluka kwa mphamvu zanu, adani anu adzabwera kwa inu mogonjera.+   Anthu onse padziko lapansi adzakugwadirani,+Ndipo adzaimba nyimbo zokutamandani, adzaimba nyimbo zotamanda dzina lanu.”+ [Seʹlah.]   Bwerani anthu inu, kuti muone ntchito za Mulungu.+Zimene wachitira ana a anthu ndi zochititsa mantha.+   Anasandutsa nyanja kukhala malo ouma,+Anthu anawoloka mtsinje mwa kuyenda ndi mapazi awo.+Pamenepo tinayamba kusangalala mwa iye.+   Iye akulamulira ndi mphamvu zake mpaka kalekale.+Maso ake akuyang’anitsitsa mitundu ya anthu.+Koma anthu oumitsa khosi asadzikweze.+ [Seʹlah.]   Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu,+Chititsani mawu omutamanda kumveka.+   Iye amatisunga ndi moyo,+Ndipo sanalole phazi lathu kupunthwa.+ 10  Pakuti inu Mulungu mwatisanthula,+Mwatiyenga ngati siliva.+ 11  Mwatilowetsa mu ukonde wosakira nyama,+Mwatinyamulitsa katundu wolemera m’chiuno mwathu. 12  Mwachititsa munthu wamba kutipondaponda.+Tadutsa pamoto ndi pamadzi,+Ndipo inu mwatipatsa mpumulo.+ 13  Ndidzalowa m’nyumba yanu ndi nsembe zopsereza zathunthu.+Ine ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa inu+ 14  Amene milomo yanga inanena,+Ndiponso amene pakamwa panga pananena nthawi imene ndinali m’masautso aakulu.+ 15  Ndidzapereka kwa inu nsembe zathunthu zopsereza za nyama zonenepa,+Pamodzi ndi nsembe zautsi wa nkhosa zamphongo.Ndidzapereka ng’ombe yamphongo pamodzi ndi mbuzi zamphongo.+ [Seʹlah.] 16  Bwerani, mvetserani, inu nonse oopa Mulungu, ndipo ine ndifotokoza+Zimene wandichitira.+ 17  Ndinamuitana ndi pakamwa panga,+Ndipo ndinamutamanda ndi lilime langa.+ 18  Ngati ndikuganizira choipa chilichonse mumtima mwanga,Yehova sadzandimvera.+ 19  Ndithudi, Mulungu wamva,+Wamvetsera mwatcheru mawu a pemphero langa.+ 20  Adalitsike Mulungu amene sananyalanyaze pemphero langa,Kapena kundimana kukoma mtima kwake kosatha.+

Mawu a M'munsi