Salimo 140:1-13

Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ya Davide. 140  Inu Yehova, ndilanditseni kwa anthu oipa.+Nditetezeni kwa munthu wochita zachiwawa,+   Anthu amene amakonza chiwembu mumtima mwawo,+Amene amandiukira tsiku lonse ngati mmene zimakhalira pankhondo.+   Anola lilime lawo ndipo lakhala ngati la njoka.+M’milomo yawo muli poizoni wa mphiri.+ [Seʹlah.]   Inu Yehova, ndithandizeni kuti manja a munthu woipa asandikhudze.+Nditetezeni kwa munthu wochita zachiwawa.+Nditetezeni kwa anthu amene andikonzera chiwembu kuti andikankhe ndi kundigwetsa.+   Anthu odzikweza anditchera msampha.+Iwo aika zingwe ponseponse ngati ukonde m’mphepete mwa njira,+Ndipo anditchera makhwekhwe.+ [Seʹlah.]   Ndauza Yehova kuti: “Inu ndinu Mulungu wanga.+Tcherani khutu, inu Yehova, ku mawu anga ochonderera.”+   Inu Yehova Ambuye Wamkulu Koposa,+ mpulumutsi wanga wamphamvu,+Mwatchinga ndi kuteteza mutu wanga pa tsiku lankhondo.+   Inu Yehova, munthu woipa musam’patse zimene mtima wake umafuna.+Musalole kuti chiwembu chawo chitheke chifukwa angadzikweze.+ [Seʹlah.]   Kunena za anthu amene andizungulira,+Zoipa zotuluka pakamwa pawo ziphimbe mitu yawo.+ 10  Muwakhuthulire makala oyaka moto pamutu pawo.+Muwachititse kugwera m’moto+ ndi m’madzi akuya kuti asanyamukenso.+ 11  Munthu wolankhula zazikulu* asakhazikike padziko lapansi.+Zoipa zisakesake munthu wochita zachiwawa ndipo zimukanthe mobwerezabwereza.+ 12  Ndikudziwa bwino kwambiri kuti Yehova adzazengera+Mlandu anthu osautsika. Iye adzachitira chilungamo anthu osauka.+ 13  Ndithudi, anthu olungama adzatamanda dzina lanu.+Anthu owongoka mtima adzakhalabe pamaso panu.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti “woneneza.” Mawu ake enieni ndi “munthu wa lilime.”