Salimo 111:1-10

111  Tamandani Ya, anthu inu!+ א [ʼAʹleph]Ndidzatamanda Yehova ndi mtima wanga wonse,+ב [Behth]Pakati pa gulu+ la owongoka mtima ndi pamsonkhano wawo.+ ג [Giʹmel]   Ntchito za Yehova ndi zazikulu,+ד [Daʹleth]Onse amene amasangalala nazo amazisinkhasinkha.+ ה [Heʼ]   Zochita zake+ n’zaulemerero ndi ulemu,+ו [Waw]Ndipo chilungamo chake chidzakhalapobe kwamuyaya.+ ז [Zaʹyin]   Iye wakonza zoti ntchito zake zodabwitsa zizikumbukiridwa.+ ח [Chehth]Yehova ndi wachisomo ndiponso wachifundo.+ ט [Tehth]   Wapereka chakudya kwa anthu omuopa.+ י [Yohdh]Iye adzakumbukira pangano lake nthawi zonse.+ כ [Kaph]   Wafotokozera anthu ake mphamvu za ntchito zake,+ל [Laʹmedh]Mwa kuwapatsa cholowa cha mitundu ina ya anthu.+ מ [Mem]   Ntchito za manja ake zimadziwika ndi choonadi ndiponso chiweruzo.+נ [Nun]Malamulo onse amene amapereka ndi odalirika.+ ס [Saʹmekh]   Ndi ochirikizika bwino mpaka muyaya, ndithu mpaka kalekale,+ע [ʽAʹyin]Ndipo amawapereka m’choonadi ndiponso molungama.+ פ [Peʼ]   Wawombola anthu ake.+ צ [Tsa·dhehʹ]Wakhazikitsa pangano lake mpaka kalekale.+ ק [Qohph]Dzina lake ndi loyera ndi lochititsa mantha.+ ר [Rehsh] 10  Chiyambi cha nzeru ndicho kuopa Yehova.+ ש [Sin]Onse otsatira malamulo a Mulungu ndi ozindikira.+ ת [Taw]Iye ayenera kutamandidwa mpaka muyaya.+

Mawu a M'munsi