Salimo 69:1-36

Kwa wotsogolera nyimbo pa Maluwa.*+ Salimo la Davide. 69  Ndipulumutseni, inu Mulungu, pakuti madzi afika m’khosi.+   Ndamila m’matope akuya, mmene mulibe malo oponda.+Ndalowa m’madzi akuya,Ndipo mtsinje wa madzi othamanga wandikokolola.+   Ndatopa ndi kufuula kwanga,+Mawu asasa pammero panga.Maso anga achita mdima poyembekezera Mulungu wanga.+   Anthu amene amadana nane popanda chifukwa achuluka kuposa tsitsi la m’mutu mwanga.+Amene akufuna kunditsitsira kuli chete, chifukwa chodana nane popanda chifukwa, achuluka kwambiri.+Ngakhale kuti sindine wakuba, anandikakamiza kubweza zinthu zimene zinabedwa.   Inu Mulungu, mwadziwa kupusa kwanga,Ndipo kupalamula kwanga sikunabisike kwa inu.+   Onse amene akuyembekezera inu asachite manyazi chifukwa cha ine,+Inu Ambuye Wamkulu Koposa, Yehova wa makamu.+Onse amene akufunafuna inu, asanyazitsidwe chifukwa cha ine,+Inu Mulungu wa Isiraeli.+   Ine ndanyamula chitonzo chifukwa cha inu,+Manyazi aphimba nkhope yanga.+   Ndadzipatula pakati pa abale anga,+Ndipo ndakhala mlendo pakati pa ana aamuna a mayi anga.+   Pakuti kudzipereka kwambiri panyumba yanu kwandidya,+Ndipo mnyozo wa anthu amene akukutonzani wagwa pa ine.+ 10  Ndipo ndinalira ndi kusala kudya chifukwa cha moyo wanga,+Koma anthu anali kungonditonza chifukwa cha zimenezo.+ 11  Pamene ndinavala ziguduli,Ndinakhala ngati mwambi kwa iwo.+ 12  Anthu okhala kuchipata anayamba kundidera nkhawa,+Ndipo anthu amene anali kumwa zakumwa zoledzeretsa anali kundinena mu nyimbo zawo.+ 13  Koma ine ndinali kupemphera kwa inu Yehova,+Pa nthawi yovomerezedwa, inu Mulungu.+Ndiyankheni mwa kuchuluka kwa kukoma mtima kwanu kosatha, ndipo sonyezani kuti ndinudi mpulumutsi.+ 14  Ndipulumutseni m’matope kuti ndisamire.+Ndipulumutseni kwa anthu odana nane+ ndiponso ku madzi akuya.+ 15  Musalole kuti mtsinje wa madzi othamanga undikokolole,+Kapena kuti madzi akuya andimize,Kapenanso kuti dzenje* lindimeze ndi kutseka pakamwa pake.+ 16  Ndiyankheni inu Yehova, pakuti kukoma mtima kwanu kosatha ndi kwabwino.+Ndicheukireni chifukwa chifundo chanu ndi chochuluka,+ 17  Ndipo ine mtumiki wanu musandibisire nkhope yanu.+Ndiyankheni mwamsanga, chifukwa ndasautsika kwambiri.+ 18  Yandikirani moyo wanga ndi kuupulumutsa.+Ndiwomboleni kwa adani anga.+ 19  Inu mwadziwa chitonzo changa, manyazi anga ndi kunyazitsidwa kwanga.+Onse odana nane ali pamaso panu.+ 20  Mtima wanga wasweka chifukwa cha chitonzo, ndipo chilonda chake ndi chosachiritsika.+Ndinali kuyembekezera kuti wina andimvere chifundo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe,+Ndinali kuyembekezera onditonthoza, koma sanapezeke ngakhale mmodzi.+ 21  Koma anandipatsa chomera chakupha kuti ndidye,+Ndipo anayesa kundimwetsa vinyo wowawasa pamene ndinali ndi ludzu.+ 22  Tebulo lawo likhale msampha,+Ndipo akodwe ndi chilichonse chimene akusangalala nacho.+ 23  Maso awo achite mdima kuti asaone,+Ndipo chititsani miyendo* yawo kunjenjemera mosalekeza.+ 24  Atsanulireni matemberero anu,+Ndipo mkwiyo woyaka moto uwagwere.+ 25  Msasa wawo wokhala ndi mpanda ukhale bwinja,+Ndipo m’mahema awo musapezeke munthu wokhalamo.+ 26  Pakuti iwo amalondalonda munthu amene inu mwamulanga,+Ndipo amakamba za ululu wa anthu amene inu mwawalasa. 27  Wonjezerani zolakwa pa zolakwa zawo,+Ndipo inu musawaone monga olungama.+ 28  Afafanizidwe m’buku la anthu amoyo,+Ndipo iwo asalembedwe m’bukumo pamodzi ndi anthu olungama.+ 29  Koma ine ndasautsika ndipo ndikumva kupweteka.+Inu Mulungu, chipulumutso chanu chinditeteze.+ 30  Ndidzatamanda dzina la Mulungu mwa kuimba nyimbo,+Ndipo ndidzamulemekeza ndi nyimbo zomuyamika.+ 31  Zimenezinso zidzasangalatsa kwambiri Yehova kuposa ng’ombe yamphongo,+Kuposa ng’ombe yamphongo yaing’ono imene ili ndi nyanga, komanso yogawanika ziboda.+ 32  Anthu ofatsa adzaona zimenezi ndipo adzakondwera.+Inu amene mukutumikira Mulungu, mtima wanu ukhalenso ndi moyo.+ 33  Pakuti Yehova akumvetsera osauka,+Ndipo sadzanyoza anthu ake amene ali m’ndende.+ 34  Kumwamba ndi dziko lapansi zimutamande,+Chimodzimodzinso nyanja ndi chilichonse choyenda mmenemo.+ 35  Pakuti Mulungu adzapulumutsa Ziyoni,+Ndipo adzamanga mizinda ya Yuda,+Iwo adzakhala mmenemo ndi kutenga dzikolo kukhala lawo.+ 36  Ana a atumiki ake adzalandira dzikolo monga cholowa chawo,+Ndipo anthu okonda dzina lake adzakhala mmenemo.+

Mawu a M'munsi

Onani mawu a m’munsi pa Sl 45:Kamutu.
Zikuoneka kuti “dzenje” limeneli ndi manda.
Mawu ake enieni, “chiuno.”