Salimo 77:1-20

Kwa wotsogolera nyimbo pa Yedutuni. Nyimbo ndi Salimo la Asafu.+ 77  Ndidzafuulira Mulungu,+Ndithu, ndidzafuulira Mulungu, ndipo iye adzatchera khutu lake kwa ine.+   Pa tsiku la zowawa zanga ndafunafuna Yehova.+Ndakweza dzanja langa kumwamba usiku wonse, ndipo silinachite dzanzi.Koma sindinatonthozeke.+   Ndidzakumbukira Mulungu ndipo ndidzavutika maganizo.+Ine ndasautsika. N’chifukwa chake ndafooka.+ [Seʹlah.]   Mwatsegula zikope zanga,+Ndipo ndavutika mtima, moti sindingathe kulankhula.+   Ndaganizira za masiku akale,+Ndaganizira zaka za makedzana.   Usiku ndidzakumbukira nyimbo zanga zoimbidwa ndi chipangizo cha zingwe.+Ndidzasonyeza kudera nkhawa mumtima mwanga,+Ndipo ndidzasinkhasinkha zinthu zonse mozama.   Kodi Yehova watitaya mpaka kalekale?+Kodi sitidzathanso kumusangalatsa?+   Kodi kukoma mtima kwake kosatha wakusiya mpaka muyaya?+Kodi malonjezo ake sadzakwaniritsidwa+ ku mibadwomibadwo?   Kodi Mulungu waiwala kukhala wokoma mtima,+Kapena watsekereza chifundo chake mwaukali?+ [Seʹlah.] 10  Kodi ndizingonena kuti: “Zimene zikundisautsa n’zakuti,+Wam’mwambamwamba wasiya kutipatsa thandizo”?+ 11  Ndidzakumbukira zochita za Ya,+Ndithu ndidzakumbukira ntchito yanu yodabwitsa yakale.+ 12  Ndidzasinkhasinkha za ntchito zanu zonse,+Ndipo ndiziganizira zochita zanu.+ 13  Inu Mulungu, njira yanu ili m’malo oyera.+Kodi ndi Mulungu wamkulu uti amene angafanane ndi Mulungu wathu?+ 14  Inu ndinu Mulungu woona amene mukuchita zodabwitsa.+Mphamvu zanu mwazidziwikitsa pakati pa mitundu ya anthu.+ 15  Ndi dzanja lanu mwawombola anthu anu,+Ana aamuna a Yakobo ndi Yosefe. [Seʹlah.] 16  Madzi akuonani, inu Mulungu,Madzi akuonani, ndipo ayamba kumva ululu woopsa.+Komanso madzi akuya ayamba kuwinduka.+ 17  Mitambo yatulutsa mabingu ndi kugwetsa madzi.+Thambo latulutsa mkokomo.Mphezi zanu zinawala paliponse ngati mivi.+ 18  Phokoso la bingu lanu linali ngati la mawilo a galeta.+Mphezi zinaunika padziko.+Ndipo dziko lapansi linagwedezeka ndi kuyamba kunjenjemera.+ 19  Msewu wanu unadutsa panyanja,+Ndipo njira yanu inadutsa pamadzi ambiri.Mmene mapazi anu anaponda simunaoneke. 20  Mwatsogolera anthu anu ngati nkhosa,+Kudzera mwa Mose ndi Aroni.+

Mawu a M'munsi