Salimo 126:1-6

Nyimbo Yokwerera Kumzinda. 126  Pamene Yehova anasonkhanitsa ndi kubwezeretsa ogwidwa ukapolo a Ziyoni,+Tinakhala ngati tikulota.+   Pa nthawiyo tinaseka kwambiri,+Ndipo lilime lathu linatulutsa mawu okondwa.+Pamenepo anthu a mitundu ina anayamba kuuzana kuti:+“Yehova wachitira anthu amenewa zinthu zazikulu.”+   Yehova watichitira zazikulu.+Tasangalala.+   Sonkhanitsani ndi kubwezeretsa gulu lathu logwidwa ukapolo inu Yehova,+Ngati mmene mumabwezeretsera madzi m’mitsinje ya ku Negebu.+   Amene akukhetsa misozi pofesa mbewu,+Adzakolola akufuula mosangalala.+   Amene akupita kumunda akulira,+Atasenza thumba lodzaza mbewu,+Adzabwerako akufuula mosangalala,+Atasenza mtolo wake wa zokolola.+

Mawu a M'munsi