Salimo 22:1-31

Kwa wotsogolera nyimbo: Nyimboyi iimbidwe motsatira Mbawala Yaikazi ya M’bandakucha. Nyimbo ya Davide. 22  Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine?+N’chifukwa chiyani mukuchedwa kundipulumutsa?+N’chifukwa chiyani simukumva mawu a kubuula kwanga?+   Inu Mulungu wanga, ine ndimaitana usana koma simundiyankha.+Usiku ndimaitanabe, moti sindikukhala chete.+   Koma inu ndinu woyera.+Mukukhala pakati pa zitamando za Isiraeli.+   Makolo athu anali kudalira inu.+Iwo anali kudalira inu ndipo munali kuwapulumutsa.+   Iwo anali kufuulira inu,+ ndipo anali kupulumuka.+Anali kudalira inu, ndipo simunawachititse manyazi.+   Koma ine ndine nyongolotsi+ osati munthu.Anthu amanditonza ndipo ndine wonyozeka kwa anthu.+   Anthu onse ondiona amandinyodola.+Iwo amandinyogodola ndi pakamwa pawo, ndipo amapukusa mitu yawo mondinyoza.+ Iwo amati:   “Anadzipereka kwa Yehova.+ Amupulumutse Iyeyo!+Ngati Mulungu amamukonda, amulanditse!”+   Pakuti ndinu amene munanditulutsa m’mimba,+Amene munandichititsa kumva kuti ndine wotetezeka pamene ndinali kuyamwa mabere a mayi anga.+ 10  Ndinaponyedwa m’manja mwanu kuchokera m’mimba.+Kuyambira ndili m’mimba mwa mayi anga, inu mwakhala Mulungu wanga.+ 11  Musakhale kutali ndi ine, chifukwa zondisautsa zili pafupi,+Ndiponso chifukwa ndilibe mthandizi winanso.+ 12  Ng’ombe zazing’ono zamphongo zochuluka zandizungulira.+Nkhunzi zamphamvu za ku Basana zandizinga.+ 13  Iwo anditsegulira pakamwa pawo mondiopseza,+Ngati mkango wokhadzula nyama umenenso ukubangula.+ 14  Ndathiridwa pansi ngati madzi.+Mafupa anga onse alekanalekana.+Mtima wanga wakhala ngati phula,+Wasungunuka mkati mwanga.+ 15  Mphamvu yanga yauma gwaa, ngati phale.+Lilime langa lamamatira kunkhama zanga,+Ndipo mwandikhazika m’fumbi la imfa.+ 16  Agalu andizungulira.+Khamu la anthu ochita zoipa landizinga.+Iwo akuluma manja ndi mapazi anga ngati mkango.+ 17  Ndingathe kuwerenga mafupa anga onse.+Adaniwo akuona zimenezi, ndipo akundiyang’anitsitsa.+ 18  Iwo akugawana zovala zanga pakati pawo,+Ndipo akuchita maere pazovala zanga.+ 19  Koma inu Yehova, musakhale kutali ndi ine,+Inu mphamvu yanga,+ ndithandizeni mofulumira.+ 20  Landitsani moyo wanga ku lupanga,+Moyo wanga wokhawu umene ndili nawo muulanditse m’kamwa mwa galu.+ 21  Ndipulumutseni m’kamwa mwa mkango,+Ndipo mundiyankhe ndi kundipulumutsa ku nyanga za ng’ombe zamphongo zam’tchire.+ 22  Ndidzalengeza dzina lanu+ kwa abale anga.+Ndidzakutamandani pakati pa mpingo.+ 23  Inu oopa Yehova, m’tamandeni!+Inu nonse mbewu ya Yakobo, m’patseni ulemerero!+Ndipo muopeni, inu nonse mbewu ya Isiraeli.+ 24  Pakuti iye sananyoze,+Kapena kunyansidwa ndi nsautso ya munthu wosautsidwa.+Ndipo sanam’bisire nkhope yake.+Pamene anamulirira kuti amuthandize, iye anamva.+ 25  Chifukwa cha zimene mwachita ndidzakutamandani mumpingo waukulu.+Ndidzakwaniritsa malonjezo anga pamaso pa anthu oopa iye.+ 26  Ofatsa adzadya ndi kukhuta.+Ofunafuna Yehova adzamutamanda.+Mitima yanu ikhale ndi moyo kosatha.+ 27  Anthu onse okhala kumalekezero a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kubwerera kwa iye.+Ndipo mafuko onse a anthu a mitundu ina adzagwada pamaso panu.+ 28  Pakuti Yehova ndiye mfumu,+Ndipo akulamulira mitundu.+ 29  Anthu onse a padziko lapansi onyada chifukwa cha chuma chawo adzadya ndi kuwerama.+Onse otsikira kufumbi adzawerama pamaso pake,+Ndipo palibe amene adzapulumutsa moyo wake.+ 30  Mbewu idzamutumikira.+Adzalengeza za Yehova ku m’badwo wotsatira.+ 31  Adzafika ndi kunena za chilungamo chake,+Adzauza anthu amene adzabadwe kuti iye ndiye wachita zimenezi.+

Mawu a M'munsi