Salimo 101:1-8

Nyimbo ndi Salimo la Davide. 101  Ndidzaimba za kukoma mtima kwanu kosatha ndi chiweruzo chanu.+Inu Yehova, ndidzakuimbirani nyimbo zokutamandani.+   Ndidzachita zinthu mwanzeru m’njira yowongoka.+Kodi inu mudzandithandiza liti?+Ndidzayendayenda m’nyumba yanga ndi mtima wanga wosagawanika.+   Sindidzaika maso anga pa chinthu chilichonse chopanda pake.+Ndimadana ndi zochita za opatuka pa choonadi.+Sindilola kuti zochita zawozo zindikhudze.+   Aliyense wopotoka maganizo amachoka pamaso panga.+Sindichita choipa chilichonse.+   Aliyense wonenera mnzake miseche,+Ndimamukhalitsa chete.+Sindingathe kupirira zochita za+Aliyense wodzikweza ndi wamtima wonyada.+   Maso anga ali pa okhulupirika a padziko lapansi,+Kuti akhale ndi ine.+Woyenda m’njira yowongoka,+Ndi amene adzanditumikira.+   M’nyumba yanga simudzakhala wochita chinyengo.+Ndipo aliyense wolankhula zachinyengo sadzapitiriza kukhala+Pamaso panga.+   M’mawa uliwonse ndidzawononga oipa onse a padziko lapansi.+Ndidzapha ndi kuchotsa mumzinda wa Yehova anthu onse ochita zinthu zopweteka anzawo.+

Mawu a M'munsi