Salimo 100:1-5

Nyimbo yoyamikira.+ 100  Fuulirani Yehova mosangalala inu nonse anthu a padziko lapansi chifukwa wapambana.+   Tumikirani Yehova mokondwera.+Bwerani kwa iye mukufuula mosangalala.+   Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu.+Iye ndi amene anatipanga, sitinadzipange tokha.+Ndife anthu ake ndi nkhosa zimene akuweta.+   Lowani pazipata zake ndi mawu oyamikira,+Lowani m’mabwalo ake ndi mawu otamanda.+Muyamikeni, tamandani dzina lake.+   Pakuti Yehova ndi wabwino.+Kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapo mpaka kalekale,+Ndipo kukhulupirika kwake kudzakhalapo ku mibadwomibadwo.+

Mawu a M'munsi