Salimo 107:1-43

(Masalimo 107 – 150) 107  Yamikani Yehova anthu inu, pakuti iye ndi wabwino.+Kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+   Anthu owomboledwa a Yehova anene zimenezi,+Anthu amene iye wawawombola m’manja mwa mdani,+   Anthu amene anawasonkhanitsa pamodzi kuchokera m’mayiko osiyanasiyana,+Kuchokera kotulukira dzuwa kukafika kolowera dzuwa,+Kuchokera kumpoto kukafika kum’mwera.+   Iwo anayendayenda m’chipululu+ mopanda kanthu.+Sanapeze njira iliyonse yopita kumzinda woti azikhalamo.+   Anali ndi njala komanso ludzu.+Anafooka kwambiri, kutsala pang’ono kufa.+   Iwo anapitiriza kufuulira Yehova m’masautso awo,+Ndipo anawalanditsa ku mavuto awo.+   Anawayendetsa m’njira yabwino,+Kuti akafike kumzinda woti azikhalamo.+   Anthu ayamike Yehova chifukwa cha kukoma mtima kwake kosatha,+Ndiponso chifukwa cha ntchito zake zodabwitsa zimene wachitira ana a anthu.+   Pakuti iye wapereka madzi kwa anthu aludzu.+Ndipo anthu anjala wawadyetsa zinthu zabwino.+ 10  Ena anali kukhala mu mdima, mu mdima wandiweyani,+Anali akaidi osautsika ndi omangidwa maunyolo,+ 11  Chifukwa anachita zinthu mopandukira+ mawu a Mulungu,+Ndipo ananyoza malangizo a Wam’mwambamwamba.+ 12  Choncho mwa kuwadzetsera mavuto, Mulungu anagonjetsa mitima yawo.+Iwo anapunthwa ndipo panalibe wowathandiza.+ 13  Iwo anayamba kuitana Yehova kuti awathandize m’masautso awo,+Ndipo iye anawapulumutsa ku mavuto awo monga mwa nthawi zonse.+ 14  Iye anawatulutsa mu mdima, mu mdima wandiweyani,+Ndi kudula zingwe zimene anamangidwa nazo.+ 15  Anthu ayamike Yehova chifukwa cha kukoma mtima kwake kosatha,+Ndiponso chifukwa cha ntchito zake zodabwitsa zimene wachitira ana a anthu.+ 16  Pakuti iye wathyola zitseko zamkuwa,+Ndipo wadula mipiringidzo yachitsulo.+ 17  Anthu amene anali opusa chifukwa cha njira yawo yophwanya malamulo,+Komanso chifukwa cha zolakwa zawo, pamapeto pake anadzibweretsera masautso.+ 18  Moyo wawo unaipidwa ndi chakudya cha mtundu uliwonse,+Ndipo anafika pazipata za imfa.+ 19  Iwo anayamba kuitana Yehova kuti awathandize m’masautso awo.+Ndipo iye anawapulumutsa ku mavuto awo monga mwa nthawi zonse.+ 20  Iye ananena mawu ndipo anawachiritsa,+Moti anawapulumutsa kudzenje la manda.+ 21  Anthu ayamike Yehova chifukwa cha kukoma mtima kwake kosatha,+Ndiponso chifukwa cha ntchito zake zodabwitsa zimene wachitira ana a anthu.+ 22  Iwo apereke nsembe zoyamikira,+Ndi kulengeza za ntchito zake ndi mfuu yachisangalalo.+ 23  Anthu amene amayenda m’zombo panyanja,+Amene amachita malonda pamadzi ambiri,+ 24  Amenewa ndi amene aona ntchito za Yehova,+Ndiponso ntchito zake zodabwitsa m’madzi akuya.+ 25  Aona mmene amautsira mphepo yamkuntho mwa kungonena mawu,+Moti nyanjayo imachita mafunde.+ 26  Iwo amapita pamwamba,Kenako amatsika pansi.Chifukwa cha masoka, mitima yawo imasungunuka.+ 27  Amadzandira ndipo amayenda peyupeyu ngati munthu woledzera,+Ndipo ngakhale nzeru zawo zonse zimasokonezeka.+ 28  Iwo amayamba kufuulira Yehova m’masautso awo,+Ndipo iye amawatulutsa m’mavuto awo.+ 29  Iye amachititsa mphepo yamkuntho kukhala bata,+Moti mafunde a panyanja amadekha.+ 30  Iwo amasangalala chifukwa mafundewo atha,Ndipo Mulungu amawatsogolera kudoko limene iwo akufuna.+ 31  Anthu ayamike Yehova chifukwa cha kukoma mtima kwake kosatha,+Ndiponso chifukwa cha ntchito zake zodabwitsa zimene wachitira ana a anthu.+ 32  Amukweze mumpingo wa anthu,+Ndipo amutamande m’bwalo la anthu achikulire.+ 33  Amasandutsa mitsinje kukhala chipululu,+Ndiponso akasupe a madzi kukhala malo opanda madzi.+ 34  Nthaka yobala zipatso amaisandutsa dziko lamchere,+Chifukwa cha kuipa kwa anthu okhala mmenemo. 35  Amasandutsa chipululu kukhala dambo la madzi,+Ndipo dziko lopanda madzi amalisintha kukhala dera la akasupe amadzi.+ 36  Kumeneko amakhazikako anthu anjala,+Kuti amange mzinda woti azikhalamo.+ 37  Anthuwo amafesa mbewu ndi kulima minda ya mpesa,+Kuti akhale ndi zokolola.+ 38  Mulungu amawadalitsa moti amachuluka kwambiri,+Ndipo salola kuti ng’ombe zawo zikhale zochepa.+ 39  Koma iwo amakhalanso ochepa ndipo amawerama,+Chifukwa cha kuponderezedwa, masoka ndi chisoni.+ 40  Mulungu akutsanulira mnyozo pa anthu olemekezeka,+Moti iye akuwachititsa kuyendayenda m’chipululu, mmene mulibe njira.+ 41  Koma akuteteza munthu wosauka ku nsautso,+Ndipo akumuchulukitsa kukhala mabanja ambiri ngati gulu la nkhosa.+ 42  Olungama amaona ndi kukondwera.+Koma anthu onse osalungama amatseka pakamwa.+ 43  Wanzeru ndani? Iye aona zimenezi,+Ndi kuchita chidwi ndi ntchito za Yehova zosonyeza kukoma mtima kwake kosatha.+

Mawu a M'munsi