Salimo 67:1-7

Kwa wotsogolera nyimbo: Nyimboyi iimbidwe ndi zipangizo za zingwe. Nyimbo ndi Salimo. 67  Mulungu adzatiyanja ndi kutidalitsa.+Iye adzatikomera mtima,+ [Seʹlah.]   Kuti njira zanu zidziwike padziko lapansi,+Kuti chipulumutso chanu chidziwike pakati pa mitundu yonse ya anthu.+   Inu Mulungu, mitundu ya anthu ikutamandeni,+Ndithu mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.+   Mitundu ya anthu isangalale ndi kufuula mokondwera,+Pakuti inu mudzaweruza anthu molungama.+Ndipo mudzatsogolera mitundu ya anthu padziko lapansi. [Seʹlah.]   Inu Mulungu, mitundu ya anthu ikutamandeni,+Ndithu mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.+   Dziko lapansi lidzapereka zipatso zake.+Mulungu, ndithu Mulungu wathu, adzatidalitsa.+   Mulungu adzatidalitsa,+Ndipo malekezero onse a dziko lapansi adzamuopa.+

Mawu a M'munsi