Salimo 8:1-9

Kwa wotsogolera nyimbo pa Gititi.*+ Nyimbo ya Davide. 8  Inu Yehova Ambuye wathu, dzina lanu ndi lalikulu padziko lonse lapansi,+Inuyo ulemerero wanu ukusimbidwa kumwambamwamba!+   M’kamwa mwa ana aang’ono ndi ana oyamwa mwakhazikitsamo zamphamvu,+Chifukwa cha amene akukuchitirani zoipa.+Mwatero kuti mugonjetse mdani wanu komanso amene akufuna kukubwezerani zoipa.+   Ndikayang’ana kumwamba, ntchito ya zala zanu,+Mwezi ndi nyenyezi zimene munapanga,+   Ndimaganiza kuti: Munthu+ ndani kuti muzimuganizira,+Ndipo mwana wa munthu wochokera kufumbi ndani kuti muzimusamalira?+   Munamuchepetsa pang’ono poyerekeza ndi ena onga Mulungu,*+Kenako munamuveka ulemerero+ ndi ulemu monga chisoti chachifumu.+   Munamupatsa mphamvu kuti alamulire ntchito za manja anu.+Mwaika zonse pansi pa mapazi ake:+   Nkhosa, mbuzi ndi ng’ombe zamphongo, zonse zimenezi,+Komanso zilombo zakutchire.+   Mbalame zam’mlengalenga ndi nsomba za m’nyanja,+Chilichonse choyenda m’njira za pansi pa nyanja.+   Inu Yehova Ambuye wathu, dzina lanu ndi lalikulu padziko lonse lapansi!+

Mawu a M'munsi

“Gititi” ndi mawu achiheberi amene anali kuwagwiritsa ntchito polemba nyimbo, koma tanthauzo lake lenileni silikudziwika.
Kapena kuti “angelo.”