Salimo 114:1-8

114  Pamene Isiraeli anatuluka mu Iguputo,+Pamene nyumba ya Yakobo inatuluka pakati pa anthu olankhula zosamveka,+   Yuda anakhala malo ake oyera,+Ndipo Isiraeli anakhala ufumu wake waukulu.+   Nyanja inaona ndipo inathawa.+Yorodano anabwerera m’mbuyo.+   Mapiri anadumphadumpha ngati nkhosa zamphongo,+Zitunda zinadumphadumpha ngati ana a nkhosa.   Kodi chinavuta n’chiyani nyanja iwe kuti uthawe?+Kodi iwe Yorodano chinavuta n’chiyani kuti ubwerere m’mbuyo?+   Nanga inu mapiri, chinavuta n’chiyani kuti mudumphedumphe ngati nkhosa zamphongo?+Inunso zitunda, chinavuta n’chiyani kuti mudumphedumphe ngati ana a nkhosa?+   Chifukwa cha Ambuye, chita mantha aakulu dziko lapansi iwe,+Chita mantha aakulu chifukwa cha Mulungu wa Yakobo,   Amene amasintha thanthwe kukhala dambo la madzi,+Ndiponso amasintha mwala wa nsangalabwi kukhala kasupe.+

Mawu a M'munsi