Mwambo Wokumbukira Imfa ya Yesu
Lachinayi 2 April 2026
A Mboni za Yehova amachita mwambo wokumbukira imfa ya Yesu kamodzi pachaka mogwirizana ndi zimene Yesu ananena kuti: “Muzichita zimenezi pondikumbukira.”—Luka 22:19.
Tikukuitanani limodzi ndi banja lanu kuti mudzabwere kumwambo umenewu.
Mafunso Amene Anthu Ambiri Amafunsa
Ndi ndani angabwere kumwambowu?
Aliyense ndi wolandiridwa. Mukhozanso kuitanira mnzanu komanso kubwera ndi anthu a m’banja lanu.
Kodi mwambowu umatenga nthawi yaitali bwanji?
Umatenga pafupifupi ola limodzi.
Kodi udzachitikira kuti?
Funsani a Mboni za Yehova kuti mudziwe kumene udzachitikire kwanuko.
Kodi mumafunika kulipira kapena kulonjeza kuti mudzapezekepo?
Ayi.
Kodi kudzakhala kuyendetsa mbale ya zopereka?
Ayi. Sitiyendetsa mbale ya zopereka pamisonkhano yathu.—Mateyu 10:8.
Kodi pali zovala zinazake zapadera zimene ndikufunika kudzavala?
Ayi. Komabe, a Mboni za Yehova amayesetsa kuvala zovala zimene zimasonyeza kuti akulemekeza mwambo wopatulikawu.
Kodi kumwambowu kuzikachitika zotani?
Tikayamba ndi kuimba nyimbo ndipo kenako wa Mboni wina akapereka pemphero loyamba. Pomalizanso tikaimba nyimbo ndipo kenako wa Mboni winanso akatseka ndi pemphero. Pamwambowu tikamvetsera nkhani yofotokoza kufunika kwa imfa ya Yesu komanso zimene tingachite kuti tipindule ndi zimene Mulungu ndi Khristu anatichitira.
Kuti mudziwe zambiri, onani nkhani yakuti “N’chifukwa Chiyani a Mboni za Yehova Mumachita Mwambo wa Mgonero wa Ambuye Mosiyana ndi Zipembedzo Zina?”
Kodi kutsogoloku ndi liti pamene Mwambo Wokumbukira Imfa ya Yesu udzachitike?
2026: Lachinayi, 2 April
2027: Lolemba, 22 March