Pitani ku nkhani yake

Mwambo Wokumbukira Imfa ya Yesu

M’madera masauzande ambiri padziko lonse lapansi, timasonkhana kuti tikumbukire imfa ya Yesu. Timachita zimenezi chifukwa chakuti iye analamula otsatira ake kuti: “Muzichita zimenezi pondikumbukira.” (Luka 22:19). Mwambo wotsatira wokumbukira imfa yake udzachitika:

Loweruka, pa 27 March 2021.

Tikukuitanani kuti mudzakhale nafe pamwambo wapadera umenewu. Chifukwa cha mliri wa kolonavairasi, mwambo wa Chikumbutso udzakhala wochita kuonera kapena kumvetsera chifukwa udzajambulidwiratu. Kuti mudziwe zoyenera kuchita kuti muonere kapena kumvetsera mwambowu, funsani wa Mboni za Yehova aliyense.