2024
Mwambo Wokumbukira Imfa ya Yesu
Kodi Nsembe Imene Anapereka Ingakuthandizeni bwanji?
Tikukuitanirani ku zochitika ziwiri izi, zomwe ndi zaulere:
-
Nkhani yapadera ya m’Baibulo yamutu wakuti “Yehova Adzagonjetsa Imfa Poukitsa Akufa”
-
Mwambo wokumbukira imfa ya Yesu
Mwambo Wokumbukira Imfa ya Yesu
Lamlungu, 24 March 2024
Kamodzi pachaka, a Mboni za Yehova amakumbukira imfa ya Yesu mogwirizana ndi zimene Yesuyo analamula kuti: “Muzichita zimenezi pondikumbukira.”—Luka 22:19.
NKHANI YAPADERA YA M’BAIBULO
“Yehova Adzagonjetsa Imfa Poukitsa Akufa”
Nkhaniyi idzakambidwa kutatsala masiku ochepa kuti mwambowu uchitike. Ndipo idzafotokoza mmene kuukitsidwa kwa anthu omwe anamwalira kungathandizire inuyo komanso okondedwa anu.
Mafunso Ofunsidwa Kawirikawiri
Kodi mwambowu udzatenga nthawi yaitali bwanji?
Udzatenga pafupifupi ola limodzi.
Kodi udzachitikira kuti?
Funsani wa Mboni za Yehova aliyense kuti mudziwe kumene udzachitikire kwanuko.
Kodi mwambowu udzakhala wolipiritsa?
Ayi.
Kodi padzakhala kuyendetsa mbale ya zopereka?
Ayi. A Mboni za Yehova samayendetsa mbale ya zopereka pamisonkhano yawo.
Kodi tidzavale zovala zotani?
Ngakhale kuti palibe zovala zapadera zomwe zimayenera kuvalidwa pamwambowu, a Mboni za Yehova amayesetsa kutsatira malangizo a m’Baibulo povala mwaulemu komanso moyenera. (1 Timoteyo 2:9) Choncho simudzafunika kuvala zovala zapadera kapena zodula.
Kodi pamwambowu padzachitika zotani?
Mwambowu udzayamba komanso kutha ndi nyimbo. Padzaperekedwanso pemphero loyamba komanso lomaliza ndi mtumiki wa Mboni za Yehova. Mbali yaikulu pamwambowu, idzakhala nkhani yomwe idzafotokoze kufunika kwa imfa ya Yesu komanso mmene tingapindulire ndi zomwe Mulungu komanso Khristu anatichitira.
Kodi Chikumbutso chotsatira chidzachitika liti?
2024: Lamlungu, 24 March
2025: Loweruka, 12 April
2026: Lachinayi, 2 April
Kuti mudziwe zambiri werengani nkhani yakuti, “N’chifukwa Chiyani a Mboni za Yehova Mumachita Mwambo wa Mgonero wa Ambuye Mosiyana ndi Zipembedzo Zina?”
Kuti mudziwe zambiri, onerani mavidiyo otsatirawa.
Muvidiyoyi muona mmene moyo udzakhalire m’tsogolo chifukwa cha imfa ya Yesu.
N’chifukwa Chiyani Yesu Anafa?
Mwina munamvapo kuti Yesu anafa chifukwa cha machimo athu. Koma kodi zingathekedi kuti imfa ya munthu mmodzi ithandize anthu mamiliyoni?
Pangani dawunilodi kapepala kosindikizidwa.