Salimo 41:1-13

Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ya Davide. 41  Wodala ndi munthu amene amachita zinthu moganizira munthu wonyozeka.+Pa tsiku la tsoka, Yehova adzamupulumutsa.+   Yehova adzamuteteza ndi kumusunga ali wamoyo.+Adzatchedwa wodala padziko lapansi.+Ndipo Mulungu sangamupereke kwa adani ake.+   Yehova adzachirikiza wonyozekayo pamene akudwala pabedi lake.+Mudzamusamalira bwino kwambiri pamene akudwala.+   Koma ine ndinati: “Inu Yehova, ndikomereni mtima.+Ndichiritseni, pakuti ndakuchimwirani.”+   Adani anga amanena zoipa zokhazokha za ine kuti:+“Kodi ameneyu afa liti kuti dzina lake lifafanizike?”   Wina akabwera kudzandiona, amalankhula zabodza kuchokera mumtima mwake.+Amasonkhanitsa nkhani zoipa.Akatero amachoka, ndipo kunjako amauza ena zabodza zokhudza ine.+   Mogwirizana, onse amene amadana nane amanong’onezana kuti andiukire.+Amandikonzera chiwembu kuti andichitire zinthu zoipa. Iwo amati:+   “Amutsanulira tsoka.*+Tsopano popeza iye wagona, sadzukanso.”+   Koma munthu amene ndinali kukhala naye mwamtendere, amene ndinali kumukhulupirira,+Munthu amene anali kudya chakudya changa,+ wakweza chidendene chake kundiukira.+ 10  Koma inu Yehova, ndikomereni mtima ndi kundidzutsa,+Kuti ndiwabwezere.+ 11  Mukatero ndidziwa kuti mwasangalala nane,Chifukwa mdani wanga sadzafuula mosangalala kuti wandipambana.+ 12  Koma ine mwandichirikiza chifukwa cha mtima wanga wosagawanika,+Ndipo mudzandiika pamaso panu mpaka kalekale.+ 13  Adalitsike Yehova Mulungu wa Isiraeli,+Kuyambira kalekale mpaka kalekale.+Ame! Ame!*+

Mawu a M'munsi

Mawu ake enieni, “chinthu chopanda pake.”
Kapena kuti “Zikhale momwemo! Zikhale momwemo!”