Salimo 127:1-5

Nyimbo ya Solomo Yokwerera Kumzinda. 127  Yehova akapanda kumanga nyumba,+Omanga nyumbayo amagwira ntchito pachabe.+Yehova akapanda kulondera mzinda,+Alonda amakhala maso pachabe.+   Anthu inu mukudzuka m’mawa pachabe,+Mukungovutika kugwira ntchito mpaka usiku,+Mukudya chakudya chimene mwachipeza movutikira.+Koma Mulungu amapereka tulo kwa wokondedwa wake.+   Taonani! Ana ndi cholowa chochokera kwa Yehova.+Chipatso cha mimba ndicho mphoto.+   Ana a bambo wachinyamata+Ali ngati mivi m’dzanja la mwamuna wamphamvu.+   Wodala ndi mwamuna wamphamvu amene wadzaza+ kachikwama kake ka mivi ndi mivi imeneyo.Abambo oterowo sadzachita manyazi,+Pakuti anawo adzalankhula ndi adani pachipata.

Mawu a M'munsi