Salimo 125:1-5

Nyimbo Yokwerera Kumzinda. 125  Okhulupirira Yehova+Ali ngati phiri la Ziyoni,+ limene silingagwedezeke, koma lidzakhalapo mpaka kalekale.+   Yehova wazungulira anthu ake+Ngati mmene mapiri azungulirira Yerusalemu,+Kuyambira tsopano mpaka kalekale.+   Ndodo yachifumu ya oipa sidzapitiriza kukhala+ padziko limene olungama analandira monga cholowa chawo,Kuti olungamawo asatambasule dzanja lawo ndi kuchita choipa.+   Inu Yehova, chitirani zabwino anthu abwino,+Anthu owongoka mtima.+   Koma anthu obwerera kunjira zawo zokhotakhota,+Yehova adzawapereka ku chilango pamodzi ndi ochita zopweteka anzawo.+Ndipo mu Isiraeli mudzakhala mtendere.+

Mawu a M'munsi