Salimo 25:1-22

Salimo la Davide. א [ʼAʹleph] 25  Ndapereka moyo wanga kwa inu Yehova.+ ב [Behth]   Inu Mulungu wanga, chikhulupiriro changa chili mwa inu.+Musalole kuti ndichite manyazi.Adani anga asakondwere chifukwa cha masautso anga.+ ג [Giʹmel]   Ndithudi, palibe aliyense amene adzachita manyazi mwa anthu amene chiyembekezo chawo chili mwa inu.+Amene adzachite manyazi ndi amene akuchita zinthu mwachinyengo koma osaphula kanthu.+ ד [Daʹleth]   Ndidziwitseni njira zanu, inu Yehova.+Ndiphunzitseni kuyenda m’njira zanu.+ ה [Heʼ]   Ndiyendetseni m’choonadi chanu ndi kundiphunzitsa,+Pakuti inu ndinu Mulungu wa chipulumutso changa.+ ו [Waw]Chiyembekezo changa chili mwa inu tsiku lonse.+ ז [Zaʹyin]   Kumbukirani chifundo chanu,+ inu Yehova, ndi zochita zanu zosonyeza kukoma mtima kosatha.+Pakuti munayamba kuchita zimenezo kale kwambiri.+ ח [Chehth]   Musakumbukire machimo a pa unyamata wanga ndi zolakwa zanga.+Ndikumbukireni malinga ndi kukoma mtima kwanu kosatha,+Ndiponso chifukwa cha ubwino wanu, inu Yehova.+ ט [Tehth]   Yehova ndi wabwino ndi wolungama.+N’chifukwa chake amalangiza ochimwa kuti ayende m’njira yoyenera.+ י [Yohdh]   Adzachititsa ofatsa kutsatira zigamulo zake,+Ndipo adzaphunzitsa ofatsa kuyenda m’njira yake.+ כ [Kaph] 10  M’njira zonse za Yehova muli kukoma mtima kosatha ndi choonadiKwa anthu osunga pangano+ lake ndi zikumbutso zake.+ ל [Laʹmedh] 11  Chifukwa cha dzina lanu, inu Yehova,+Mundikhululukire cholakwa changa ngakhale kuti n’chachikulu.+ מ [Mem] 12  Tsopano munthu woopa Yehova ndani?+Adzamulangiza kuyenda m’njira imene adzasankha.+ נ [Nun] 13  Moyo wake udzasangalala ndi ubwino wa Mulungu,+Mbadwa zake zidzatenga dziko lapansi kukhala lawo.+ ס [Saʹmekh] 14  Ubwenzi wolimba ndi Yehova ndi wa anthu amene amamuopa,+Pangano lakenso ndi la anthu oterowo, ndipo iye amawadziwitsa panganolo.+ ע [ʽAʹyin] 15  Maso anga amayang’ana kwa Yehova nthawi zonse,+Chifukwa iye ndi amene amawonjola phazi langa mu ukonde.+ פ [Peʼ] 16  Ndicheukireni ndi kundikomera mtima.+Pakuti ndasungulumwa ndipo ndasautsika.+ צ [Tsa·dheh] 17  Masautso a mtima wanga awonjezeka.+Ndilanditseni ku nkhawa zimene zili pa ine.+ ר [Rehsh] 18  Onani masautso anga ndi mavuto anga,+Ndipo mundichotsere machimo anga onse.+ 19  Onani mmene adani anga achulukira,+Ndipo chifukwa cha chidani chawo chachikulu, amafuna kundichitira chiwawa.+ ש [Shin] 20  Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa.+Musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndathawira kwa inu.+ ת [Taw] 21  Mtima wanga wosagawanika ndiponso wowongoka unditeteze,+Pakuti chiyembekezo changa chili mwa inu.+ 22  Inu Mulungu, wombolani Isiraeli m’masautso ake onse.+

Mawu a M'munsi