Salimo 91:1-16

91  Aliyense wokhala m’malo otetezeka+ a Wam’mwambamwamba+Adzakhala wosungika mumthunzi wa Wamphamvuyonse.+   Ndidzauza Yehova kuti: “Inu ndinu pothawirapo panga ndi malo anga achitetezo,+Mulungu wanga amene ndimamukhulupirira.”+   Pakuti iye adzakupulumutsa mumsampha wa wosaka mbalame,+Ndi ku mliri wobweretsa masautso.+   Adzakutchinjiriza ndi mapiko ake,+Udzathawira pansi pa mapiko ake.+Choonadi chake+ chidzakhala chishango chako+ chachikulu ndi malo ako achitetezo.   Usiku sudzaopa choopsa chilichonse,+Ndipo sudzaopanso muvi+ woponyedwa masana,   Sudzaopa mliri umene umayenda mu mdima,+Kapena chiwonongeko chimene chimachitika dzuwa lili paliwombo.+   Anthu 1,000 adzagwa pambali pako,Ndipo anthu 10,000 adzagwa kudzanja lako lamanja.Koma palibe zoterezi zimene zidzakuchitikira.+   Udzayang’ana ndi maso ako,+Ndipo udzaona anthu oipa akulandira chilango.+   Popeza wanena kuti: “Yehova ndiye pothawirapo panga,”+Wapanga Wam’mwambamwamba kukhala malo ako okhalamo.+ 10  Palibe tsoka limene lidzakugwera,+Ndipo ngakhale mliri sudzayandikira hema wako.+ 11  Pakuti adzalamula angelo ake za iwe,+Kuti akuteteze m’njira zako zonse.+ 12  Iwo adzakunyamula m’manja mwawo,+Kuti phazi lako lisawombe mwala uliwonse.+ 13  Udzapondaponda mkango wamphamvu ndi njoka ya mamba,+Ndipo udzapondaponda mkango wamphamvu kwambiri ndi chinjoka.+ 14  Mulungu wanena kuti: “Popeza wasonyeza kuti amandikonda,+Inenso ndidzamupulumutsa.+Ndidzamuteteza chifukwa wadziwa dzina langa.+ 15  Adzandiitana ndipo ndidzamuyankha.+Ndidzakhala naye m’nthawi ya masautso.+Ndidzamupulumutsa ndi kumupatsa ulemerero.+ 16  Ndidzamukhutiritsa ndi masiku ambiri,+Ndipo ndidzamuonetsa chipulumutso changa.”+

Mawu a M'munsi