Salimo 64:1-10

Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ya Davide. 64  Inu Mulungu, imvani mawu ofotokoza nkhawa zanga.+Tetezani moyo wanga kuti usaope mdani.+   Ndibiseni kuti ndisamve zinsinsi za anthu ochita zoipa,+Kuti ndisamve phokoso la anthu ochita zovulaza anzawo,+   Amene anola lilime lawo ngati lupanga,+Amene alunjikitsa mivi yawo, imene ndi mawu awo owawa,+   Pa munthu wosalakwa, kuti amulase atamubisalira.+Amamulasa modzidzimutsa ndipo saopa.+   Amaumirira kulankhula zoipa,+Amakambirana kuti atchere misampha.+Iwo amati: “Angaione ndani?”+   Amafunafuna kuchita zinthu zosalungama,+Abisa chiwembu chimene achikonza mochenjera,+Ndipo zamkati, zamumtima mwa aliyense, n’zovuta kuzimvetsa.+   Koma Mulungu adzawalasa ndi muvi modzidzimutsa.+Iwo adzakhala ndi zilonda,+   Ndipo iwo amakhumudwitsa munthu,+Koma lilime lawo likutsutsana nawo.+Onse owayang’ana adzapukusa mitu yawo,+   Anthu onse adzachita mantha,+Ndipo adzanena za ntchito za Mulungu,+Iwo adzamvetsa bwino ntchito zake.+ 10  Wolungama adzakondwera mwa Yehova ndipo adzathawira kwa iye,+Ndipo onse owongoka mtima adzatamanda Mulungu.+

Mawu a M'munsi