Salimo 64:1-10

  • Nditetezeni ku ziwembu zobisika

    • “Mulungu adzawalasa” (7)

Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ya Davide. 64  Inu Mulungu, imvani mawu anga pamene ndikukuchondererani.+ Tetezani moyo wanga ku zinthu zoopsa zimene mdani akuchita.  2  Ndibiseni ku ziwembu zachinsinsi za anthu oipa,+Kwa gulu la anthu ochita zoipa.  3  Iwo amanola lilime lawo ngati lupanga.Amakonzekera kuponya mawu awo opweteka ngati mivi,  4  Kuti alase munthu wosalakwa atamubisalira.Amamulasa modzidzimutsa ndiponso mopanda mantha.  5  Amaumirira kuti akwaniritse zolinga zawo zoipa,*Amakambirana zimene angachite kuti abise misampha yawo. Iwo amanena kuti: “Angaione ndani?”+  6  Amafufuza njira zatsopano zochitira zinthu zoipa.Mwachinsinsi amakonza njira zochitira ziwembu zawo mochenjera.+Zimene munthu aliyense akuganiza mumtima mwake, nʼzovuta kuzimvetsa.  7  Koma Mulungu adzawalasa ndi muvi.+Adzavulazidwa ndi muvi modzidzimutsa.  8  Adzawonongedwa chifukwa cha zolankhula za lilime lawo lomwe,+Onse amene adzaone zimenezi adzapukusa mitu yawo.  9  Ndiyeno anthu onse adzachita mantha,Ndipo adzalengeza zimene Mulungu wachita,Iwo adzamvetsa bwino zimene iye amachita.+ 10  Wolungama adzasangalala chifukwa cha Yehova ndipo adzathawira kwa iye.+Onse owongoka mtima adzasangalala kwambiri.*

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “Amalimbikitsana kuti achite zoipa.”
Kapena kuti, “adzadzitamandira.”