Salimo 14:1-7

  • Zimene opusa amachita

    • “Kulibe Yehova” (1)

    • “Palibe aliyense amene akuchita zabwino” (3)

Kwa wotsogolera nyimbo. Salimo la Davide. 14  Munthu wopusa* amanena mumtima mwake kuti: “Kulibe Yehova.”+ Zochita za anthu amenewa ndi zoipa komanso zonyansa,Ndipo palibe amene akuchita zabwino.+  2  Koma kuchokera kumwamba, Yehova amayangʼana ana a anthu,Kuti aone ngati pali aliyense wozindikira, ngati pali aliyense amene akufunafuna Yehova.+  3  Onse apatuka,+Ndipo onsewo ndi achinyengo. Palibe aliyense amene akuchita zabwino,Palibiretu ndi mmodzi yemwe.  4  Kodi palibe aliyense womvetsa zinthu pakati pa anthu ochita zoipawa? Iwo amadya anthu anga ngati kuti akudya chakudya. Ndipo sapemphera kwa Yehova.  5  Koma adzagwidwa ndi mantha aakulu,+Chifukwa Yehova ali pakati pa mʼbadwo wa anthu olungama.  6  Inu anthu ochita zoipa mumayesetsa kusokoneza mapulani a munthu wonyozeka,Koma Yehova ndi malo ake othawirako.+  7  Zikanakhala bwino chipulumutso cha Isiraeli chikanachokera ku Ziyoni.+ Yehova akadzabwezeretsa anthu ake amene anagwidwa nʼkutengedwa kupita kudziko lina,Yakobo adzasangalale, Isiraeli adzakondwere.

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “wopanda nzeru.”