Salimo 121:1-8

  • Yehova amateteza anthu ake

    • “Thandizo langa limachokera kwa Yehova” (2)

    • Yehova samagona (3, 4)

Nyimbo Yokwerera Kumzinda. 121  Ndakweza maso anga kuyangʼana kumapiri.+ Kodi thandizo langa lichokera kuti?  2  Thandizo langa limachokera kwa Yehova,+Amene anapanga kumwamba ndi dziko lapansi.  3  Iye sadzalola kuti phazi lako literereke.*+ Amene akukuyangʼanira sadzawodzera.  4  Taonani! Amene akuyangʼanira Isiraeli,+Sadzawodzera kapena kugona.  5  Yehova akukuyangʼanira. Yehova ndi mthunzi+ wako kudzanja lako lamanja.+  6  Masana dzuwa silidzakupweteka,+Kapenanso mwezi usiku.+  7  Yehova adzakuteteza ku zinthu zonse zimene zingakuvulaze.+ Iye adzateteza moyo wako.+  8  Yehova adzakuteteza pa zochita zako zonse,*Kuyambira panopa mpaka kalekale.

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “lipunthwe.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “pamene ukutuluka komanso pamene ukulowa.”