Salimo 149:1-9
149 Tamandani Ya!*
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,+Mutamandeni mumpingo wa anthu ake okhulupirika.+
2 Isiraeli asangalale ndi Mlengi wake Wamkulu.+Ana a Ziyoni akondwere ndi Mfumu yawo.
3 Atamande dzina lake akuvina+Komanso kumuimbira nyimbo zomutamanda pogwiritsa ntchito maseche ndi zeze.+
4 Chifukwa Yehova amasangalala ndi anthu ake.+
Iye amakongoletsa anthu ofatsa ndi chipulumutso.+
5 Anthu okhulupirika asangalale chifukwa Mulungu amawalemekeza.Iwo aimbe mosangalala ali pamabedi awo.+
6 Pakamwa pawo patuluke nyimbo zotamanda Mulungu,Ndipo lupanga lakuthwa konsekonse likhale mʼmanja mwawo,
7 Kuti abwezere anthu a mitundu ina,Komanso kupereka chilango kwa mitundu ya anthu,
8 Ndiponso kuti amange mafumu awo maunyolo,Komanso kumanga anthu awo olemekezeka mʼmatangadza achitsulo.
9 Kuti awalange mogwirizana ndi chigamulo chimene chinalembedwa.+
Ulemerero umenewu ndi wa anthu onse okhulupirika a Mulungu.
Tamandani Ya!*
Mawu a M'munsi
^ Kapena kuti, “Aleluya.” “Ya” ndi chidule cha dzina lakuti Yehova.
^ Kapena kuti, “Aleluya.” “Ya” ndi chidule cha dzina lakuti Yehova.