Salimo 80:1-19

  • Anapempha Mʼbusa wa Isiraeli kuti awabwezeretse mwakale

    • “Inu Mulungu, tibwezeretseni mwakale” (3)

    • Isiraeli ali ngati mtengo wampesa wa Mulungu (8-15)

Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimboyi iimbidwe motsatira kaimbidwe ka “Nyimbo ya Maluwa.” Chikumbutso. Nyimbo ndi Salimo la Asafu.+ 80  Inu Mʼbusa wa Isiraeli, mvetserani,Inu amene mukutsogolera Yosefe ngati gulu la nkhosa.+ Inu amene mwakhala pampando wachifumu pamwamba* pa akerubi,+Onetsani kuwala kwanu.*  2  Sonyezani mphamvu zanu+Pa Efuraimu, Benjamini ndi Manase.Bwerani mudzatipulumutse.+  3  Inu Mulungu, tibwezeretseni mwakale.+Walitsani nkhope yanu pa ife kuti tipulumutsidwe.+  4  Inu Yehova Mulungu wa magulu ankhondo akumwamba, kodi mudzakwiyira* anthu anu nʼkukana kumvetsera mapemphero awo mpaka liti?+  5  Mwawapatsa misozi kuti ikhale chakudya chawo,Ndipo mukuwamwetsa misozi yochuluka kwambiri.  6  Mwachititsa kuti anthu oyandikana nafe azikanganirana ifeyo.Adani athu akupitirizabe kutinyoza mmene akufunira.+  7  Inu Mulungu wa magulu ankhondo akumwamba, tibwezeretseni mwakale.Walitsani nkhope yanu pa ife kuti tipulumutsidwe.+  8  Munachititsa kuti mtengo wa mpesa+ uchoke mu Iguputo. Munathamangitsa mitundu ya anthu kuti mudzalemo mtengowo.+  9  Munalambula malo odzalapo mtengo wa mpesawo,Ndipo unazika mizu nʼkudzaza dziko.+ 10  Mapiri anaphimbika ndi mthunzi wake,Ndipo mitengo yamkungudza ya Mulungu inaphimbika ndi nthambi zake. 11  Nthambi zake zinakafika mpaka kunyanja,Ndipo mphukira zake zinafika ku Mtsinje.*+ 12  Nʼchifukwa chiyani mwagwetsa mpanda wamiyala wa munda wampesawo,+Kuti anthu onse odutsa mumsewu azithyola zipatso zake?+ 13  Nguluwe zamʼnkhalango zikuwononga mtengowo,Ndipo nyama zakutchire zikuudya.+ 14  Inu Mulungu wa magulu ankhondo akumwamba, chonde bwererani. Yangʼanani pansi pano muli kumwambako kuti muone, Ndipo samalirani mtengo wa mpesa uwu,+ 15  Mtengo umene dzanja lanu lamanja ladzala.+Ndipo muone mwana wanu amene munamupatsa* mphamvu kuti inu mulemekezeke.+ 16  Wawotchedwa ndi moto+ nʼkudulidwa. Anthu amawonongeka ndi kudzudzula kwanu.* 17  Dzanja lanu lithandize munthu amene ali kudzanja lanu lamanja,Lithandize mwana wa munthu amene mwamupatsa mphamvu kuti mulemekezeke.+ 18  Mukatero ife sitidzakusiyani. Tithandizeni kuti tikhalebe ndi moyo kuti titamande dzina lanu. 19  Inu Yehova Mulungu wa magulu ankhondo akumwamba, tibwezeretseni mwakale.Walitsani nkhope yanu pa ife kuti tipulumutsidwe.+

Mawu a M'munsi

Mabaibulo ena amati, “pakati.”
Kapena kuti, “Onetsani kunyezimira kwanu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mudzalusira.”
Umenewu ndi mtsinje wa Firate.
Kapena kuti, “nthambi imene munaipatsa.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “kudzudzula kwa nkhope yanu.”