Salimo 22:1-31

  • Kuchoka mʼmavuto nʼkuyamba kutamanda Mulungu

    • “Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine?” (1)

    • “Akuchita maere pa zovala zanga” (18)

    • Tamandani Mulungu mumpingo (22,25)

    • Dziko lonse lilambire Mulungu (27)

Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimboyi iimbidwe motsatira “Mbawala Yaikazi ya Mʼbandakucha.”* Nyimbo ya Davide. 22  Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine?+ Nʼchifukwa chiyani mukuchedwa kundipulumutsa?Nʼchifukwa chiyani simukumva kubuula kwanga?+  2  Inu Mulungu wanga, ine ndimakuitanani masana, koma simundiyankha.+Ndipo usiku sindikhala chete, ndimaitanabe.  3  Koma inu ndinu woyera,+Ndipo mwazunguliridwa ndi* mawu otamanda a Isiraeli.  4  Makolo athu ankadalira inu.+Iwo ankakudalirani ndipo inu munkawapulumutsa.+  5  Iwo ankafuulira inu ndipo munkawapulumutsa.Ankakudalirani ndipo simunawakhumudwitse.*+  6  Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu,Anthu amandinyogodola* komanso kundinyoza.+  7  Anthu onse amene amandiona amandiseka.+Iwo amandinyogodola nʼkumapukusa mitu yawo mondinyoza nʼkumati:+  8  “Anadzipereka kwa Yehova. Tiyeni tione ngati angamupulumutse! Musiyeni Mulungu amupulumutse, chifukwa amamukonda kwambiri!”+  9  Inu ndi amene munanditulutsa mʼmimba,+Ndinu amene munandichititsa kumva kuti ndine wotetezeka pamene ndinkayamwa mabere a mayi anga. 10  Ndinaperekedwa kwa inu kuti muzindisamalira* kuyambira pamene ndinabadwa.Kuyambira ndili mʼmimba mwa mayi anga, inu mwakhala Mulungu wanga. 11  Musakhale kutali ndi ine, chifukwa mavuto ali pafupi+Ndipo palibe winanso amene angandithandize.+ 12  Ngʼombe zazingʼono zamphongo zochuluka zandizungulira.+Ngʼombe zamphongo zamphamvu za ku Basana zandizungulira.+ 13  Iwo atsegula pakamwa pawo nʼkumandiopseza,+Ngati mkango wobangula umene umakhadzulakhadzula nyama.+ 14  Ndathiridwa pansi ngati madzi.Mafupa anga onse aguluka. Mtima wanga wakhala ngati phula,+Ukusungunuka mkati mwanga.+ 15  Mphamvu zanga zauma ngati phale.+Lilime langa lamatirira kunkhama zanga,+Ndipo mwandilowetsa mʼdzenje kuti ndife.+ 16  Adani anga andizungulira ngati agalu.+Andizungulira ngati gulu la anthu ochita zoipa,+Mofanana ndi mkango, iwo akundiluma manja ndi mapazi.+ 17  Ndingathe kuwerenga mafupa anga onse.+ Adaniwo akuona zimenezi ndipo akundiyangʼanitsitsa. 18  Iwo akugawana zovala zanga,Ndipo akuchita maere pa zovala zanga.+ 19  Koma inu Yehova, musakhale kutali ndi ine.+ Inu ndinu mphamvu zanga, ndithandizeni mofulumira.+ 20  Ndipulumutseni ku lupanga,Pulumutsani moyo wanga wamtengo wapatali* mʼkamwa* mwa agalu.+ 21  Ndipulumutseni mʼkamwa mwa mkango+ komanso kunyanga za ngʼombe zamphongo zamʼtchire.Mundiyankhe ndi kundipulumutsa. 22  Ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga.+Ndidzakutamandani pakati pa mpingo.+ 23  Inu amene mumaopa Yehova, mutamandeni! Inu nonse mbadwa* za Yakobo, mʼpatseni ulemerero!+ Muopeni, inu nonse mbadwa* za Isiraeli. 24  Chifukwa iye sananyoze kapena kunyansidwa ndi kuvutika kwa munthu woponderezedwa.+Sanabise nkhope yake kwa iye.+ Pamene anamulirira kuti amuthandize, iye anamva.+ 25  Ndidzakutamandani mumpingo waukulu.+Ndidzakwaniritsa malonjezo anga pamaso pa anthu amene amamuopa. 26  Ofatsa adzadya nʼkukhuta.+Anthu amene akufunafuna Yehova adzamutamanda.+ Musangalale ndi moyo* mpaka kalekale. 27  Anthu onse ochokera kumalekezero a dziko lapansi adzakumbukira Yehova nʼkupita kwa iye. Ndipo mabanja onse a mitundu ya anthu adzagwada pamaso panu.+ 28  Chifukwa Yehova ndi Mfumu,+Ndipo akulamulira mitundu ya anthu. 29  Anthu onse olemera* padziko lapansi adzadya ndipo adzamuweramira.Anthu onse amene amabwerera kufumbi adzagwada pamaso pake,Ndipo palibe aliyense wa iwo amene angapulumutse moyo wawo. 30  Mbadwa* zawo zidzamutumikira.Mibadwo yamʼtsogolo idzauzidwa zokhudza Yehova. 31  Adzabwera nʼkunena za chilungamo chake. Adzauza anthu amene adzabadwe zimene iye wachita.

Mawu a M'munsi

Nʼkutheka kuti chimenechi chinali chuni kapena mtundu wa kaimbidwe.
Kapena kuti, “mpando wanu wachifumu uli pakati pa.”
Kapena kuti, “simunawachititse manyazi.”
Kapena kuti, “amandichitira zachipongwe.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Anandiponyera kwa inu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “wokhawu umene ndili nawo,” kutanthauza moyo wake.
Mʼchilankhulo choyambirira, “mʼmanja.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mbewu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mbewu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Mtima wanu ukhale ndi moyo.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “onenepa.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mbewu.”