Salimo 132:1-18
Nyimbo Yokwerera Kumzinda.
132 Inu Yehova, kumbukirani DavideKomanso mavuto onse amene anakumana nawo.+
2 Kumbukirani kuti analumbira kwa inu Yehova,Analonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti:+
3 “Sindidzalowa mutenti yanga, mʼnyumba yanga.+
Sindidzagona pabedi langa.
4 Sindidzalola kuti ndigoneKapena kutseka maso anga,
5 Mpaka nditamupezera Yehova malo okhala,Malo abwino oti* Wamphamvu wa Yakobo azikhalamo.”+
6 Ku Efurata,+ tinamva zimene zinachitika.Tinalipeza kunkhalango.*+
7 Tiyeni tilowe mʼmalo ake okhala.*+Tiyeni tiwerame pachopondapo mapazi ake.+
8 Nyamukani, inu Yehova, kuti mulowe mʼmalo anu okhalamo,+Inu pamodzi ndi Likasa limene likuimira mphamvu zanu.+
9 Ansembe anu avale chilungamo,Ndipo okhulupirika anu afuule mosangalala.
10 Chifukwa cha zimene munalonjeza Davide mtumiki wanu,Musakane* wodzozedwa wanu.+
11 Yehova walumbira kwa Davide.Ndithudi sadzalephera kukwaniritsa mawu ake akuti:
“Ndidzaika pampando wako wachifumuMmodzi wa ana ako.*+
12 Ana ako akadzasunga pangano langaKomanso malamulo* anga amene ndikuwaphunzitsa,+Ana awonsoAdzakhala pampando wako wachifumu kwamuyaya.”+
13 Chifukwa Yehova wasankha Ziyoni.+Akufunitsitsa kuti akhale malo ake okhalamo. Iye akuti:+
14 “Awa ndi malo anga okhalamo mpaka kalekale.Ndidzakhala mmenemu,+ chifukwa zimenezi ndi zimene ndikulakalaka.
15 Ndidzadalitsa kwambiri malo amenewa ndi chakudya.Anthu ake osauka ndidzawapatsa chakudya chokwanira.+
16 Ansembe ake ndidzawaveka chipulumutso,+Ndipo okhulupirika ake adzafuula mosangalala.+
17 Kumeneko ndidzachulukitsa mphamvu* za Davide.
Wodzozedwa wanga ndamukonzera nyale.+
18 Adani ake ndidzawaveka manyazi,Koma ufumu wake udzakhala wamphamvu.”*+
Mawu a M'munsi
^ Kapena kuti, “Chihema chachikulu choti.”
^ Nʼkutheka kuti akunena zokhudza Likasa.
^ Kapena kuti, “tilowe mʼchihema chake chachikulu.”
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “Musabweze nkhope ya.”
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “Chipatso cha mimba yako.”
^ Kapena kuti, “zikumbutso.”
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “nyanga.”
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “chisoti chake chachifumu chidzakhala champhamvu.”