Salimo 52:1-9
Kwa wotsogolera nyimbo. Masikili.* Salimo la Davide, pa nthawi imene Doegi wa ku Edomu, anapita kwa Sauli nʼkukamuuza kuti Davide wapita kunyumba ya Ahimeleki.+
52 Nʼchifukwa chiyani ukudzitukumula chifukwa cha zinthu zoipa zimene ukuchita, wamphamvu iwe?+
Chikondi chokhulupirika cha Mulungu nʼchokhalitsa.+
2 Lilime lako limene ndi lakuthwa ngati lezala,+Limakonza chiwembu komanso kuchita zachinyengo.+
3 Umakonda kwambiri zinthu zoipa kuposa zabwino,Umakonda kwambiri kunama kuposa kulankhula zoona. (Selah)
4 Umakonda mawu onse opweteka ena,Iwe amene lilime lako limalankhula zachinyengo.
5 Nʼchifukwa chake Mulungu adzakugwetsa ndipo sudzakhalakonso.+Adzakugwira nʼkukukokera kutali ndi tenti yako,+Ndipo adzakuzula nʼkukuchotsa mʼdziko la anthu amoyo.+ (Selah)
6 Olungama adzaona zimenezi nʼkuchita mantha,+Ndipo adzamuseka+ kuti:
7 “Taonani, munthu uyu sanadalire Mulungu monga malo ake othawirako,*+Koma ankadalira chuma chake chochuluka,+Komanso ziwembu zimene ankapanga.”*
8 Koma ine ndidzakhala ngati mtengo waukulu wa maolivi wa masamba obiriwira mʼnyumba ya Mulungu.Ndidzadalira chikondi chokhulupirika cha Mulungu+ mpaka kalekale.
9 Ndidzakutamandani mpaka kalekale, chifukwa cha zimene mwachita.+Pamaso pa okhulupirika anu,Ndidzayembekezera dzina lanu,+ chifukwa ndi labwino.
Mawu a M'munsi
^ Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
^ Kapena kuti, “achitetezo.”
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “mavuto amene ankayambitsa.”