Salimo 16:1-11

  • Zabwino zonse zimachokera kwa Yehova

    • “Yehova ndi gawo langa” (5)

    • ‘Maganizo amumtima mwanga amandiuza zoyenera kuchita’ (7)

    • ‘Yehova ali kudzanja langa lamanja’ (8)

    • “Simudzandisiya mʼManda” (10)

Mikitamu* ya Davide. 16  Nditetezeni, inu Mulungu, chifukwa ndathawira kwa inu.+  2  Ndauza Yehova kuti: “Inu ndinu Yehova. Zinthu zonse zabwino pa moyo wanga zimachokera kwa inu.*  3  Ndipo oyera amene ali padziko lapansi,Anthu aulemerero amenewo, ndi amene amandichititsa kukhala wosangalala kwambiri.”+  4  Anthu amene amafunitsitsa kulambira milungu ina amachulukitsa chisoni chawo.+ Ine sindidzapereka nsembe zachakumwa za magazi kwa milungu ina,Ndipo milomo yanga sidzatchula mayina awo.+  5  Yehova ndi gawo langa, gawo limene ndinapatsidwa+ komanso kapu yanga.+ Inu mumateteza cholowa changa.  6  Malo amene andiyezera ndi abwino kwambiri. Inde, ndikukhutira ndi cholowa chimene ndapatsidwa.+  7  Ndidzatamanda Yehova amene wandipatsa malangizo.+ Ngakhale usiku maganizo amkati mwa mtima wanga* amandiuza zoyenera kuchita.+  8  Ndimaika Yehova patsogolo panga nthawi zonse.+ Chifukwa iye ali kudzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.*+  9  Choncho mtima wanga ukusangalala, ndikusangalala kwambiri.* Ndipo ndikukhala motetezeka. 10  Chifukwa simudzandisiya* mʼManda.*+ Simudzalola kuti wokhulupirika wanu aone dzenje.*+ 11  Mumandidziwitsa njira ya moyo.+ Ndikakhala nanu pafupi,* ndimasangalala kwambiri.+Kudzanja lanu lamanja kuli chimwemwe* mpaka kalekale.

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “Ubwino wanga umachokera kwa inu.”
Kapena kuti, “mmene ndikumvera mumtima mwanga.” Mʼchilankhulo choyambirira, “impso zanga.”
Kapena kuti, “sindidzadzandira.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “ulemerero wanga ukusangalala.”
Kapena kuti, “simudzasiya moyo wanga.”
Amenewa ndi manda a anthu onse. Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Mabaibulo ena amati, “avunde.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ndikakhala pafupi ndi nkhope yanu.”
Kapena kuti, “chisangalalo.”