Salimo 23:1-6

  • “Yehova ndi Mʼbusa wanga”

    • “Sindidzasowa kanthu” (1)

    • “Amanditsitsimula” (3)

    • “Kapu yanga ndi yodzaza bwino” (5)

Nyimbo ya Davide. 23  Yehova ndi Mʼbusa wanga.+ Sindidzasowa kanthu.+  2  Amandigoneka mʼmalo odyetsera ziweto a msipu wambiri.Amanditsogolera kumalo opumira a madzi ambiri.*+  3  Amanditsitsimula.*+ Amanditsogolera munjira zachilungamo chifukwa cha dzina lake.+  4  Ngakhale ndikuyenda mʼchigwa chamdima wandiweyani,+Sindikuopa kanthu,+Chifukwa inu muli ndi ine.+Chibonga chanu ndi ndodo yanu zikundipangitsa kumva kuti ndine wotetezeka.*  5  Mumandipatsa chakudya patebulo pamaso pa adani anga.+ Ndimatsitsimulidwa mukandidzoza mafuta kumutu.+Kapu yanga ndi yodzaza bwino.+  6  Ndithu, masiku onse a moyo wanga ndidzasangalala ndi ubwino wanu komanso chikondi chanu chokhulupirika,+Ndipo ndidzakhala mʼnyumba ya Yehova kwa moyo wanga wonse.+

Mawu a M'munsi

Mabaibulo ena amati, “a madzi odikha.”
Kapena kuti, “Amatsitsimula moyo wanga.”
Kapena kuti, “Chibonga chanu ndi ndodo yanu zimandilimbikitsa.”