Salimo 119:1-176

  • Kuyamikira mawu amtengo wapatali a Mulungu

    • “Kodi wachinyamata angakhale bwanji woyera pa moyo wake?” (9)

    • “Ndimakonda kwambiri zikumbutso zanu” (24)

    • “Mawu anu ndi chiyembekezo changa” (74,81,114)

    • “Ndimakonda kwambiri chilamulo chanu!” (97)

    • “Wozindikira kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse” (99)

    • “Mawu anu ndi nyale younikira kumapazi anga” (105)

    • “Mawu anu onse ndi choonadi chokhachokha” (160)

    • Amene amakonda chilamulo cha Mulungu amakhala ndi mtendere (165)

א [Aleph] 119  Osangalala ndi anthu amene salakwitsa kanthu* mʼnjira zawo,Amene amatsatira chilamulo cha Yehova.+  2  Osangalala ndi anthu amene amasunga zikumbutso zake,+Amene amamufunafuna ndi mtima wawo wonse.+  3  Iwo sachita zinthu zosalungama.Amayenda mʼnjira zake.+  4  Inu mwalamulaKuti tizitsatira malamulo anu mosamala.+  5  Zikanakhala bwino ndikanakhala wolimba*+Kuti nditsatire malangizo anu.  6  Zikanatero sindikanachita manyazi,+Pa nthawi imene ndikuganizira malamulo anu onse.  7  Ndidzakutamandani ndi mtima wowongoka,Pamene ndikuphunzira zigamulo zanu zolungama.  8  Ndidzasunga malangizo anu. Choncho musandisiye ndekha. ב [Beth]  9  Kodi wachinyamata angakhale bwanji woyera pa moyo wake? Akamadzifufuza nthawi zonse kuti aone ngati zochita zake zikugwirizana ndi mawu anu.+ 10  Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse. Musalole kuti ndisochere nʼkuchoka pa malamulo anu.+ 11  Ndasunga mosamala mawu anu mumtima mwanga+Kuti ndisakuchimwireni.+ 12  Mutamandike, inu Yehova.Ndiphunzitseni malamulo anu. 13  Ndi milomo yanga ndalengezaZigamulo zonse zimene inu mwanena. 14  Ndimasangalala ndi zikumbutso zanu,+Kuposa mmene ndimasangalalira ndi zinthu zina zonse zamtengo wapatali.+ 15  Ndidzaganizira mozama* malamulo anu,+Ndipo ndidzayangʼanitsitsa njira zanu.+ 16  Ndimakonda malamulo anu. Sindidzaiwala mawu anu.+ ג [Gimel] 17  Ndichitireni zinthu mokoma mtima, ine mtumiki wanu,Kuti ndikhale ndi moyo komanso kuti ndisunge mawu anu.+ 18  Tsegulani maso anga kuti ndione bwinobwinoZinthu zodabwitsa zamʼchilamulo chanu. 19  Ine ndine mlendo mʼdzikoli.+ Musandibisire malamulo anu. 20  Ndimalakalaka kwambiriNditadziwa zigamulo zanu nthawi zonse. 21  Mumadzudzula anthu odzikuza,Otembereredwa amene akusochera nʼkusiya kutsatira malamulo anu.+ 22  Muwachititse kuti asiye* kusandilemekeza komanso kundinyoza,Chifukwa ndatsatira zikumbutso zanu. 23  Ngakhale pamene akalonga asonkhana pamodzi nʼkumakambirana zoti andiukire,Ine mtumiki wanu ndimaganizira mozama* malangizo anu. 24  Ndimakonda kwambiri zikumbutso zanu,+Ndipo zili ngati anthu amene amandipatsa malangizo.+ ד [Daleth] 25  Ndagona pafumbi.+ Ndithandizeni kuti ndikhalebe ndi moyo mogwirizana ndi mawu anu.+ 26  Ndinakuuzani za njira zanga ndipo munandiyankha.Ndiphunzitseni malamulo anu.+ 27  Ndithandizeni kumvetsa tanthauzo la* malamulo anu,Kuti ndiganizire mozama* ntchito zanu zodabwitsa.+ 28  Ine ndakhala ndikusowa tulo chifukwa cha chisoni. Ndilimbitseni mogwirizana ndi mawu anu. 29  Ndithandizeni kuti ndisakhale munthu wachinyengo,+Ndipo mundikomere mtima pondipatsa chilamulo chanu. 30  Ine ndasankha kuti ndizichita zinthu mokhulupirika.+ Ndimadziwa kuti zigamulo zanu ndi zolungama. 31  Ndimatsatira zikumbutso zanu nthawi zonse.+ Inu Yehova, musalole kuti ndikhumudwe.*+ 32  Ndidzatsatira* malamulo anu ndi mtima wonse,Chifukwa mwandithandiza kuti ndiwamvetse bwino. ה [He] 33  Ndiphunzitseni inu Yehova,+ kuti ndizichita zinthu mogwirizana ndi malangizo anu,Ndipo ndidzawatsatira kwa moyo wanga wonse.+ 34  Ndithandizeni kuti ndikhale wozindikiraKuti nditsatire chilamulo chanu,Ndiponso kuti ndichisunge ndi mtima wanga wonse. 35  Nditsogolereni* mʼnjira ya malamulo anu,+Chifukwa njira imeneyi imandisangalatsa 36  Ndithandizeni kuti mtima wanga uzikonda zikumbutso zanu,Osati kupeza phindu mwachinyengo.+ 37  Ndithandizeni kuti ndizipewa kuyangʼana zinthu zopanda pake.+Ndithandizeni kuyenda mʼnjira yanu kuti ndikhalebe ndi moyo. 38  Kwaniritsani zimene munalonjeza* mtumiki wanu,Kuti anthu azikuopani. 39  Chotsani zinthu zochititsa manyazi zimene ndikuziopa,Chifukwa zigamulo zanu ndi zabwino.+ 40  Taonani mmene ndikulakalakira malamulo anu. Ndithandizeni kukhalabe ndi moyo mogwirizana ndi chilungamo chanu. ו [Waw] 41  Ndione chikondi chanu chokhulupirika, inu Yehova,+Komanso mundipulumutse mogwirizana ndi lonjezo lanu.*+ 42  Mukatero ndiyankha amene akundinyoza,Chifukwa ine ndimadalira mawu anu. 43  Ndithandizeni kuti ndipitirize kunena mawu a choonadi,Chifukwa ndikuyembekezera* chigamulo chanu. 44  Ndidzasunga chilamulo chanu nthawi zonse,Mpaka kalekale.+ 45  Ndidzayendayenda mʼmalo otetezeka,*+Chifukwa ndimayesetsa kuphunzira malamulo anu. 46  Ndidzanena zokhudza zikumbutso zanu pamaso pa mafumu,Ndipo sindidzachita manyazi.+ 47  Ndimakonda kwambiri malamulo anu,Inde, ndimawakonda.+ 48  Ndidzapemphera kwa inu nditakweza manja anga chifukwa ndimakonda malamulo anu,+Ndipo ndidzaganizira mozama* malangizo anu.+ ז [Zayin] 49  Kumbukirani mawu amene* munandiuza ine mtumiki wanu,Mawu amene mumandipatsa nawo chiyembekezo.* 50  Izi ndi zimene zimandilimbikitsa ndikakhala pamavuto,+Chifukwa mawu anu andithandiza kuti ndikhalebe ndi moyo. 51  Anthu odzikuza andinyoza koopsa.Koma ine sindinasiye kutsatira chilamulo chanu.+ 52  Ndimakumbukira zigamulo zanu zakalekale+ inu Yehova,Ndipo zimandilimbikitsa.+ 53  Ndakwiya kwambiri chifukwa cha oipa,Amene akusiya chilamulo chanu.+ 54  Kwa ine, malangizo anu ali ngati nyimbo,Kulikonse kumene ndimakhala.* 55  Usiku ndimakumbukira dzina lanu, inu Yehova,+Kuti ndisunge chilamulo chanu. 56  Ndakhala ndikuchita zimeneziChifukwa ndimatsatira malamulo anu. ח [Heth] 57  Yehova ndi cholowa changa.+Ndalonjeza kusunga mawu anu.+ 58  Ndikukupemphani* ndi mtima wanga wonse.+Ndikomereni mtima+ mogwirizana ndi zimene munalonjeza.* 59  Ndaganizira mozama za njira zanga,Kuti mapazi anga ndiwabwezere ku zikumbutso zanu.+ 60  Ndimafulumira ndipo sindizengerezaKusunga malamulo anu.+ 61  Zingwe za oipa zandikulunga,Koma ine sindinaiwale chilamulo chanu.+ 62  Ndimadzuka pakati pa usiku kuti ndikuyamikeni+Chifukwa cha zigamulo zanu zolungama. 63  Ine ndine mnzawo wa anthu amene amakuopani,Ndiponso wa anthu amene amasunga malamulo anu.+ 64  Inu Yehova, chikondi chanu chokhulupirika chadzaza dziko lapansi.+Ndiphunzitseni malamulo anu. ט [Teth] 65  Inu Yehova, mwandichitira zabwino ine mtumiki wanu,Mogwirizana ndi mawu anu. 66  Ndithandizeni kuti ndikhale wozindikira komanso wodziwa zinthu,+Chifukwa ndimadalira malamulo anu. 67  Ndisanakumane ndi mavuto ndinkasochera pafupipafupi,*Koma panopa ndimasunga mawu anu.+ 68  Inu ndinu wabwino+ ndipo ntchito zanu ndi zabwino. Ndiphunzitseni malamulo anu.+ 69  Anthu odzikuza akundinenera zinthu zambiri zabodza,Koma ine ndimasunga malamulo anu ndi mtima wanga wonse. 70  Mitima yawo yauma ngati mwala,*+Koma ine ndimakonda kwambiri chilamulo chanu.+ 71  Zili bwino kuti ndakumana ndi mavuto,+Kuti ndiphunzire malamulo anu. 72  Chilamulo chimene mwapereka nʼchabwino kwa ine,+Nʼchabwino kwambiri kuposa ndalama zagolide ndi zasiliva masauzande ambiri.+ י [Yod] 73  Manja anu anandipanga komanso kundiumba. Ndithandizeni kuti ndikhale wozindikira,Kuti ndiphunzire malamulo anu.+ 74  Amene amakuopani amasangalala akandiona,Chifukwa mawu anu ndi chiyembekezo changa.*+ 75  Inu Yehova, ndikudziwa kuti zigamulo zanu ndi zolungama+Komanso kuti mwandilanga chifukwa chakuti ndinu wokhulupirika.+ 76  Chikondi chanu chokhulupirika+ chindilimbikitse,Mogwirizana ndi zimene munandilonjeza* ine mtumiki wanu. 77  Ndisonyezeni chifundo kuti ndipitirize kukhala ndi moyo,+Chifukwa ndimakonda kwambiri chilamulo chanu.+ 78  Odzikuza achite manyazi,Chifukwa amandilakwira popanda chifukwa. Koma ine ndidzaganizira mozama* malamulo anu.+ 79  Anthu amene amakuopani abwerere kwa ine,Amene amadziwa zikumbutso zanu. 80  Mtima wanga uzitsatira malangizo anu mosalakwitsa kanthu,+Kuti ndisachite manyazi.+ כ [Kaph] 81  Ine ndikulakalaka chipulumutso chanu,+Chifukwa mawu anu ndi chiyembekezo changa.* 82  Maso anga akulakalaka mawu anu+Ndipo ndikunena kuti: “Kodi mudzandilimbikitsa liti?”+ 83  Chifukwa ndili ngati thumba lachikopa limene lauma mu utsi,Koma sindinaiwale malangizo anu.+ 84  Kodi ine mtumiki wanu ndidikira mpaka liti? Kodi anthu amene akundizunza mudzawaweruza liti?+ 85  Anthu odzikuza andikumbira dzenje kuti ndigweremo,Anthu amene safuna kutsatira chilamulo chanu. 86  Malamulo anu onse ndi odalirika. Anthu akundizunza popanda chifukwa. Chonde, ndithandizeni.+ 87  Iwo anangotsala pangʼono kundifafaniza padziko lapansi,Koma ine sindinasiye kutsatira malamulo anu. 88  Ndithandizeni kuti ndikhalebe ndi moyo chifukwa cha chikondi chanu chokhulupirika,Kuti ndisunge zikumbutso zimene mwatipatsa. ל [Lamed] 89  Inu Yehova, mawu anu adzakhazikika kumwamba,+Mpaka kalekale. 90  Kukhulupirika kwanu kudzakhalapobe ku mibadwo yonse.+ Mwakhazikitsa mwamphamvu dziko lapansi, kuti lipitirizebe kukhalapo.+ 91  Ntchito zanu zilipobe mpaka pano chifukwa cha zigamulo zanu,Chifukwa zonsezo zimakutumikirani. 92  Ndikanakhala kuti sindimakonda kwambiri chilamulo chanu,Ndikanakhala nditafa chifukwa cha mavuto anga.+ 93  Sindidzaiwala malamulo anu,Chifukwa mwandithandiza kuti ndikhalebe ndi moyo pogwiritsa ntchito malamulo amenewo.+ 94  Ine ndine wanu. Chonde ndipulumutseni,+Chifukwa ndimayesetsa kuphunzira malamulo anu.+ 95  Oipa amayembekezera kuti andiwononge,Koma ine ndimamvetsera mwatcheru zikumbutso zanu. 96  Ndaona kuti zinthu zonse zabwino kwambiri zili ndi malire,Koma malamulo anu alibe malire.* מ [Mem] 97  Ndimakonda kwambiri chilamulo chanu!+ Ndimaganizira mozama* chilamulocho tsiku lonse.+ 98  Malamulo anu amandichititsa kukhala wanzeru kuposa adani anga,+Chifukwa ali ndi ine mpaka kalekale. 99  Ndine wozindikira kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse,+Chifukwa ndimaganizira mozama* zikumbutso zanu. 100  Ndimachita zinthu mozindikira kuposa anthu achikulire,Chifukwa ndimatsatira malamulo anu. 101  Ndimakana kuyenda mʼnjira iliyonse yoipa,+Kuti ndisunge mawu anu. 102  Sindinasiye kutsatira zigamulo zanu,Chifukwa inu mwandilangiza. 103  Mawu anu amatsekemera kwambiri mʼkamwa mwanga,Kuposa mmene uchi umakomera!+ 104  Ndimachita zinthu mozindikira chifukwa cha malamulo anu.+ Nʼchifukwa chake ndimadana ndi njira iliyonse yachinyengo.+ נ [Nun] 105  Mawu anu ndi nyale younikira kumapazi anga,Komanso kuwala kounikira njira yanga.+ 106  Ndalumbira kuti ndidzasunga zigamulo zanu zolungama,Ndipo ndidzakwaniritsa lumbiro langa. 107  Ndavutika kwambiri.+ Inu Yehova, ndithandizeni kuti ndikhalebe ndi moyo mogwirizana ndi mawu anu.+ 108  Inu Yehova, chonde sangalalani ndi nsembe zanga zaufulu zokutamandani,*+Ndipo mundiphunzitse zigamulo zanu.+ 109  Nthawi zonse moyo wanga umakhala pangozi,*Koma sindinaiwale chilamulo chanu.+ 110  Oipa anditchera msampha,Koma ine sindinasochere nʼkusiya kutsatira malamulo anu.+ 111  Ndimaona kuti zikumbutso zanu ndi chuma changa mpaka kalekale,*Chifukwa zimasangalatsa mtima wanga.+ 112  Ndatsimikiza mtima kumvera malamulo anuNthawi zonse, mpaka ndidzamwalire. ס [Samekh] 113  Ndimadana ndi anthu amitima iwiri,+Koma ndimakonda chilamulo chanu.+ 114  Inu ndinu malo anga obisalamo komanso chishango changa,+Chifukwa mawu anu ndi chiyembekezo changa.*+ 115  Mukhale kutali ndi ine, anthu oipa inu,+Kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga. 116  Inu Mulungu, ndithandizeni mogwirizana ndi zimene munalonjeza,*+Kuti ndikhalebe ndi moyo.Musalole kuti ndichite manyazi chifukwa cha chiyembekezo changa.*+ 117  Ndithandizeni kuti ndipulumutsidwe.+Mukatero ndidzamvera malangizo anu nthawi zonse.+ 118  Onse amene amasochera nʼkusiya kutsatira malangizo anu mumawakana,+Chifukwa ndi abodza komanso achinyengo. 119  Anthu onse oipa apadziko lapansi mumawataya ngati zinthu zopanda ntchito zimene zimatsalira poyenga zitsulo.+ Nʼchifukwa chake ine ndimakonda zikumbutso zanu. 120  Chifukwa choopa inu, thupi langa limanjenjemera.Ndikuopa zigamulo zanu. ע [Ayin] 121  Ndachita zinthu zachilungamo komanso zoyenera. Musandipereke kwa anthu amene amandipondereza. 122  Lonjezani kuti mudzandithandiza ine mtumiki wanu.Musalole kuti anthu odzikuza andipondereze. 123  Maso anga afooka chifukwa choyembekezera chipulumutso chanu+Komanso malonjezo* anu olungama.+ 124  Ndisonyezeni chikondi chanu chokhulupirika ine mtumiki wanu,+Ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.+ 125  Ine ndine mtumiki wanu. Ndithandizeni kukhala wozindikira,+Kuti ndidziwe zikumbutso zanu. 126  Nthawi yoti Yehova achitepo kanthu yakwana,+Chifukwa iwo aphwanya chilamulo chanu. 127  Nʼchifukwa chake ine ndimakonda malamulo anuKuposa golide, ngakhale golide wabwino kwambiri.*+ 128  Choncho ndimaona kuti malangizo* onse ochokera kwa inu ndi abwino.+Ndimadana ndi njira iliyonse yachinyengo.+ פ [Pe] 129  Zikumbutso zanu nʼzodabwitsa. Nʼchifukwa chake ine ndimazitsatira. 130  Mawu anu akafotokozedwa amathandiza munthu kuti akhale wozindikira,+Amathandiza munthu wosadziwa zambiri kuti akhale wozindikira.+ 131  Ndatsegula kwambiri pakamwa panga kuti ndiuse moyo,*Chifukwa ndikulakalaka malamulo anu.+ 132  Ndiyangʼaneni ndipo mundikomere mtima,+Mogwirizana ndi zigamulo zimene mumapereka kwa anthu amene amakonda dzina lanu.+ 133  Nditsogolereni ndi mawu anu kuti ndiyende mʼnjira yotetezeka.Musalole kuti choipa chilichonse chindilamulire.+ 134  Ndipulumutseni* kwa anthu amene akundipondereza,Ndipo ine ndidzasunga malamulo anu. 135  Chititsani nkhope yanu kuti indiwalire* ine mtumiki wanu,+Ndipo mundiphunzitse malamulo anu. 136  Misozi ikutsika mʼmaso mwanga ngati mtsinjeChifukwa anthu sakusunga chilamulo chanu.+ צ [Tsade] 137  Ndinu wolungama, inu Yehova,+Ndipo zigamulo zanu ndi zachilungamo.+ 138  Zikumbutso zimene mumapereka ndi zolungamaKomanso nʼzodalirika kwambiri. 139  Kudzipereka kwanga kwa inu kuli ngati moto umene ukuyaka mumtima mwanga,+Chifukwa adani anga aiwala mawu anu. 140  Mawu anu ndi oyengeka bwino kwambiri,+Ndipo ine mtumiki wanu ndimawakonda.+ 141  Anthu ena amandiona ngati wopanda ntchito komanso wonyozeka.+Komabe sindinaiwale malamulo anu. 142  Chilungamo chanu chidzakhalapo mpaka kalekale,+Ndipo chilamulo chanu ndi choonadi.+ 143  Ngakhale kuti ndikukumana ndi zowawa komanso mavuto,Ndikupitirizabe kukonda malamulo anu. 144  Zikumbutso zanu zidzakhalabe zolungama mpaka kalekale. Ndithandizeni kukhala wozindikira+ kuti ndikhalebe ndi moyo. ק [Qoph] 145  Ndaitana ndi mtima wanga wonse. Ndiyankheni inu Yehova. Ndidzatsatira malangizo anu. 146  Ndakuitanani. Ndipulumutseni chonde! Ndidzasunga zikumbutso zanu. 147  Ndadzuka mʼbandakucha kuti ndipemphe thandizo kwa inu,+Chifukwa mawu anu ndi chiyembekezo changa.* 148  Ndimadzuka pakati pa usiku,*Kuti ndiganizire mozama* mawu anu.+ 149  Imvani mawu anga chifukwa cha chikondi chanu chokhulupirika.+ Inu Yehova, ndithandizeni kuti ndikhalebe ndi moyo mogwirizana ndi chilungamo chanu. 150  Anthu amene amakonda kuchita khalidwe lochititsa manyazi* abwera pafupi ndi ine.Iwo ndi otalikirana kwambiri ndi chilamulo chanu. 151  Inu Yehova muli pafupi,+Ndipo malamulo anu onse ndi choonadi.+ 152  Kale kwambiri, ndinaphunzira zokhudza zikumbutso zanu,Kuti munazikhazikitsa kuti zikhalepo mpaka kalekale.+ ר [Resh] 153  Onani mavuto anga ndipo mundipulumutse,+Chifukwa sindinaiwale chilamulo chanu. 154  Nditetezeni pa mlandu wanga* ndipo mundipulumutse.+Ndithandizeni kuti ndikhalebe ndi moyo mogwirizana ndi lonjezo lanu.* 155  Chipulumutso chili kutali kwambiri ndi anthu oipa,Chifukwa sanaphunzire malamulo anu.+ 156  Chifundo chanu nʼchachikulu, inu Yehova.+ Ndithandizeni kuti ndikhalebe ndi moyo mogwirizana ndi chilungamo chanu. 157  Anthu ondizunza komanso adani anga ndi ambiri.+Koma ine sindinasiye kutsatira zikumbutso zanu. 158  Ndimanyansidwa ndi anthu ochita zinthu mwachinyengo,Chifukwa sasunga mawu anu.+ 159  Onani mmene ndimakondera malamulo anu. Inu Yehova, ndithandizeni kuti ndikhalebe ndi moyo chifukwa cha chikondi chanu chokhulupirika.+ 160  Mawu anu onse ndi choonadi chokhachokha,+Ndipo zigamulo zanu zonse zolungama zidzakhalapo mpaka kalekale. ש [Sin] kapena kuti [Shin] 161  Akalonga amandizunza+ popanda chifukwa,Koma mtima wanga umaopa mawu anu.+ 162  Ndimasangalala ndi mawu anu,+Mofanana ndi munthu amene wapeza chuma chambiri. 163  Ndimadana ndi chinyengo ndipo chimandinyansa,+Ndimakonda chilamulo chanu.+ 164  Ndimakutamandani maulendo 7 pa tsiku,Chifukwa cha zigamulo zanu zolungama. 165  Anthu amene amakonda chilamulo chanu amakhala ndi mtendere wochuluka,+Palibe chimene chingawakhumudwitse.* 166  Ndimayembekezera ntchito zanu zachipulumutso, inu Yehova,Ndipo ndimatsatira malamulo anu. 167  Ndimasunga zikumbutso zanu,Ndipo ndimazikonda kwambiri.+ 168  Ndimasunga malamulo anu ndi zikumbutso zanu,Chifukwa inu mukudziwa zinthu zonse zimene ndimachita.+ ת [Taw] 169  Inu Yehova, imvani kulira kwanga kopempha thandizo.+ Ndithandizeni kuti ndikhale wozindikira, mogwirizana ndi mawu anu.+ 170  Pempho langa lakuti mundikomere mtima lifike kwa inu. Ndipulumutseni mogwirizana ndi zimene munalonjeza.* 171  Milomo yanga isefukire ndi mawu okutamandani,+Chifukwa mumandiphunzitsa malamulo anu. 172  Lilime langa liimbe zokhudza mawu anu,+Chifukwa malamulo anu onse ndi olungama. 173  Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza,+Chifukwa ndasankha kumvera malamulo anu.+ 174  Ndikulakalaka chipulumutso chanu, inu Yehova,Ndipo ndimakonda kwambiri chilamulo chanu.+ 175  Ndithandizeni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni,+Zigamulo zanu zindithandize. 176  Ndasochera ngati nkhosa yotayika.+ Ndifunefuneni ine mtumiki wanu,Chifukwa sindinaiwale malamulo anu.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “amachita zinthu mokhulupirika.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “njira zanga zikanakhala zokhazikika.”
Kapena kuti, “Ndidzaphunzira.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Mugubuduze nʼkundichotsera.”
Kapena kuti, “Ine mtumiki wanu ndimaphunzira.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “njira za.”
Kapena kuti, “ndiphunzire.”
Kapena kuti, “ndichite manyazi.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ndidzathamanga mʼnjira za.”
Kapena kuti, “Ndiyendetseni.”
Kapena kuti, “munauza.”
Kapena kuti, “mawu anu.”
Kapena kuti, “ndikudikirira.”
Kapena kuti, “mʼmalo otakasuka.”
Kapena kuti, “Ndipo ndidzaphunzira.”
Kapena kuti, “lonjezo limene.”
Kapena kuti, “Mawu amene munachititsa kuti ndiziwayembekezera.”
Kapena kuti, “Mʼnyumba imene ndimakhala monga mlendo.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ndafewetsa nkhope yanu kuti mundimwetulire.”
Kapena kuti, “mawu anu.”
Kapena kuti, “ndinkachimwa mosadziwa.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “yauma ngati mafuta oundana.”
Kapena kuti, “Chifukwa ndikuyembekezera mawu anu.”
Kapena kuti, “Mogwirizana ndi mawu anu.”
Kapena kuti, “ine ndidzaphunzira.”
Kapena kuti, “Chifukwa ndikuyembekezera mawu anu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “amakhudza mbali zonse.”
Kapena kuti, “Ndimaphunzira.”
Kapena kuti, “Chifukwa ndimaphunzira.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “nsembe zaufulu za pakamwa panga.”
Kapena kuti, “Nthawi zonse moyo wanga umakhala mʼdzanja langa.”
Kapena kuti, “ndi cholowa changa chamuyaya.”
Kapena kuti, “Chifukwa ndikuyembekezera mawu anu.”
Kapena kuti, “mogwirizana ndi mawu anu.”
Kapena kuti, “chiyembekezo changa chindichititse manyazi.”
Kapena kuti, “mawu.”
Kapena kuti, “woyenga bwino.”
Kapena kuti, “malamulo.”
Kapena kuti, “kuti ndipumire mʼmwamba.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ndiwomboleni.”
Kapena kuti, “indimwetulire.”
Kapena kuti, “Chifukwa ndikuyembekezera mawu anu.”
Kapena kuti, “Ndimadzuka maulonda a usiku asanathe.”
Kapena kuti, “Kuti ndiphunzire.”
Kapena kuti, “khalidwe lonyansa.”
Kapena kuti, “Ndiweruzireni mlandu wanga.”
Kapena kuti, “mawu anu.”
Kapena kuti, “Kwa iwo palibe chopunthwitsa.”
Kapena kuti, “mogwirizana ndi mawu anu.”