Salimo 84:1-12

  • Kulakalaka chihema chachikulu cha Mulungu

    • Mlevi ankalakalaka atakhala ngati mbalame (3)

    • “Tsiku limodzi mʼmabwalo anu” (10)

    • “Mulungu ndi dzuwa ndiponso chishango” (11)

Kwa wotsogolera nyimbo, pa Gititi.* Nyimbo ndi Salimo la ana a Kora.+ 84  Inu Yehova wa magulu ankhondo akumwamba,Ine ndimakonda kwambiri chihema chanu chachikulu!+  2  Moyo wanga ukulakalaka kwambiri,Inde, ndafookeratu chifukwa cholakalakaMabwalo a Yehova.+ Mtima wanga ndi thupi langa zikufuula mosangalala kwa Mulungu wamoyo.  3  Ngakhale mbalame zapeza malo okhala kumenekoNdipo namzeze wadzimangira chisa chake,Mmene amasamaliramo ana akePafupi ndi guwa lanu lansembe lalikulu, inu Yehova wa magulu ankhondo akumwamba,Mfumu yanga ndi Mulungu wanga!  4  Osangalala ndi anthu amene akukhala mʼnyumba yanu!+ Iwo akupitiriza kukutamandani.+ (Selah)  5  Osangalala ndi anthu amene amapeza mphamvu kuchokera kwa inu,+Amene mitima yawo imalakalaka misewu yaikulu yopita kunyumba yanu.  6  Akamadutsa mʼchigwa cha Baka,*Amasandutsa chigwacho kukhala malo opezeka akasupe.Ndipo mvula yoyambirira imabweretsa madalitso mʼchigwacho.  7  Mphamvu zawo zidzapitiriza kuwonjezeka pamene akuyenda.+Aliyense wa iwo amaonekera pamaso pa Mulungu mu Ziyoni.  8  Inu Yehova Mulungu wa magulu ankhondo akumwamba, imvani pemphero langa.Mvetserani, inu Mulungu wa Yakobo. (Selah)  9  Inu Mulungu wathu komanso chishango chathu,+ onani,*Yangʼanani nkhope ya wodzozedwa wanu.+ 10  Kukhala tsiku limodzi mʼmabwalo anu nʼkwabwino kuposa kukhala kwinakwake masiku 1,000!+ Ndasankha kuima pakhomo la nyumba ya Mulungu wangaKuposa kukhala mʼmatenti a anthu oipa. 11  Chifukwa Yehova Mulungu ndi dzuwa+ ndiponso chishango.+Iye amatikomera mtima nʼkutipatsa ulemerero. Yehova sadzalephera kupereka chinthu chilichonse chabwinoKwa anthu amene amachita zinthu mokhulupirika.+ 12  Inu Yehova wa magulu ankhondo akumwamba,Wosangalala ndi munthu amene amakukhulupirirani.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “mʼchigwa cha zitsamba za baka.”
Mabaibulo ena amati, “Yangʼanani chishango chathu, Inu Mulungu.”