Salimo 75:1-10

  • Mulungu amaweruza mwachilungamo

    • Anthu oipa adzamwa zamʼkapu ya Yehova (8)

Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimboyi iimbidwe motsatira kaimbidwe ka nyimbo yakuti “Musandiwononge.” Nyimbo ndi Salimo la Asafu.+ 75  Timakuyamikani, inu Mulungu, timakuyamikani.Dzina lanu lili pafupi ndi ife,+Ndipo anthu akulengeza ntchito zanu zodabwitsa.  2  Inu mukuti: “Ndikasankha nthawi yoti ndiweruze,Ndimaweruza mwachilungamo.  3  Pamene dziko lapansi ndi onse okhala mmenemo ananjenjemera* ndi mantha,Ine ndi amene ndinalimbitsa zipilala zake.” (Selah)  4  Anthu odzitukumula ndinawauza kuti, “Musadzitukumule,” Ndipo oipa ndinawauza kuti, “Musadzikuze chifukwa choti muli ndi mphamvu.*  5  Musadzikuze chifukwa choti muli ndi mphamvu*Kapena kulankhula mwamatama.  6  Chifukwa ulemu wa munthu suchokeraKumʼmawa, kumadzulo kapena kumʼmwera.  7  Mulungu ndiye woweruza.+ Amatsitsa munthu wina nʼkukweza wina.+  8  Mʼdzanja la Yehova muli kapu.+Vinyo akuchita thovu ndipo wasakanizidwa bwino. Ndithudi, iye adzakhuthula vinyo yenseNdipo anthu onse oipa padziko lapansi adzamwa mpaka kugugudiza nsenga zake.”+  9  Koma ine ndidzalengeza zimenezi mpaka kalekale.Ndidzaimba nyimbo zotamanda Mulungu wa Yakobo. 10  Mulungu akuti: “Ndidzathetsa mphamvu* zonse za anthu oipa,Koma ndidzachititsa kuti mphamvu* za anthu olungama zionekere bwino.”

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “anasungunuka.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Musakweze nyanga yanu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Musakweze nyanga yanu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “nyanga.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “nyanga.”