Salimo 70:1-5

  • Anapempha kuti amuthandize mwamsanga

    • “Ndithandizeni mwamsanga” (5)

Kwa wotsogolera nyimbo. Salimo la Davide. Nyimbo ya chikumbutso. 70  Inu Mulungu, ndipulumutseni,Inu Yehova, ndithandizeni mofulumira.+  2  Amene akufuna kuchotsa moyo wangaAchititsidwe manyazi komanso anyozeke. Amene akusangalala ndi tsoka langaAbwerere mwamanyazi.  3  Onse amene akunena kuti: “Eyaa! Eyaa!” Abwezedwe mwamanyazi.  4  Koma amene akufunafuna inu,Akondwere ndi kusangalala chifukwa choti akudziwani.+ Amene amasangalala ndi njira imene mumapulumutsira anthu, nthawi zonse azinena kuti: “Mulungu alemekezeke.”  5  Koma ine ndine munthu wovutika komanso wosauka.+Inu Mulungu, ndithandizeni mwamsanga.+ Inu ndi amene mumandithandiza komanso kundipulumutsa.+Inu Yehova musachedwe.+

Mawu a M'munsi